< Yobu 38 >
1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Then the LORD answered Job out of the whirlwind, and said:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Who is this that darkeneth counsel by words without knowledge?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Gird up now thy loins like a man; for I will demand of thee, and declare thou unto Me.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Where wast thou when I laid the foundations of the earth? Declare, if thou hast the understanding.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Who determined the measures thereof, if thou knowest? Or who stretched the line upon it?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Whereupon were the foundations thereof fastened? Or who laid the corner-stone thereof,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
When the morning stars sang together, and all the sons of God shouted for joy?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Or who shut up the sea with doors, when it broke forth, and issued out of the womb;
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
When I made the cloud the garment thereof, and thick darkness a swaddlingband for it,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
And prescribed for it My decree, and set bars and doors,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
And said: 'Thus far shalt thou come, but no further; and here shall thy proud waves be stayed'?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Hast thou commanded the morning since thy days began, and caused the dayspring to know its place;
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
That it might take hold of the ends of the earth, and the wicked be shaken out of it?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
It is changed as clay under the seal; and they stand as a garment.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
But from the wicked their light is withholden, and the high arm is broken.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Hast thou entered into the springs of the sea? Or hast thou walked in the recesses of the deep?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Have the gates of death been revealed unto thee? Or hast thou seen the gates of the shadow of death?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Hast thou surveyed unto the breadths of the earth? Declare, if thou knowest it all.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Where is the way to the dwelling of light, and as for darkness, where is the place thereof;
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
That thou shouldest take it to the bound thereof, and that thou shouldest know the paths to the house thereof?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Thou knowest it, for thou wast then born, and the number of thy days is great!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Hast thou entered the treasuries of the snow, or hast thou seen the treasuries of the hail,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Which I have reserved against the time of trouble, against the day of battle and war?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
By what way is the light parted, or the east wind scattered upon the earth?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Who hath cleft a channel for the waterflood, or a way for the lightning of the thunder;
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
To cause it to rain on a land where no man is, on the wilderness, wherein there is no man;
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
To satisfy the desolate and waste ground, and to cause the bud of the tender herb to spring forth?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Hath the rain a father? Or who hath begotten the drops of dew?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Out of whose womb came the ice? And the hoar-frost of heaven, who hath gendered it?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
The waters are congealed like stone, and the face of the deep is frozen.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Canst thou bind the chains of the Pleiades, or loose the bands of Orion?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Canst thou lead forth the Mazzaroth in their season? Or canst thou guide the Bear with her sons?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Knowest thou the ordinances of the heavens? Canst thou establish the dominion thereof in the earth?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Canst thou lift up thy voice to the clouds, that abundance of waters may cover thee?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Canst thou send forth lightnings, that they may go, and say unto thee: 'Here we are'?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Who hath put wisdom in the inward parts? Or who hath given understanding to the mind?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Who can number the clouds by wisdom? Or who can pour out the bottles of heaven,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
When the dust runneth into a mass, and the clods cleave fast together?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Wilt thou hunt the prey for the lioness? Or satisfy the appetite of the young lions,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
When they couch in their dens, and abide in the covert to lie in wait?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Who provideth for the raven his prey, when his young ones cry unto God, and wander for lack of food?