< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Nu nam Jahweh het woord, en sprak tot Job in de storm:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Wie zijt gij, die de Voorzienigheid duister maakt Door woorden zonder verstand?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Omgord uw lenden als een man, Ik zal u vragen stellen, gij moogt Mij leren!
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Waar waart ge, toen Ik de aarde grondde: Vertel het, zo ge er iets van weet!
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Wie heeft haar grootte bepaald: gij weet het zo goed; Wie het meetsnoer over haar gespannen?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Waarop zijn haar zuilen geplaatst, Of wie heeft haar hoeksteen gelegd:
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
Onder het gejuich van het koor der morgensterren, Het jubelen van de zonen Gods?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Wie heeft de zee achter deuren gesloten, Toen zij bruisend uit de moederschoot kwam;
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
Toen Ik haar de wolken gaf als een kleed, De nevel als haar windsels;
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
Toen Ik haar grenzen heb gesteld, Slagboom en grendels haar gaf;
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
Toen Ik sprak: Ge komt tot hier en niet verder, Hier wordt de trots van uw golven gebroken!
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Hebt gij ooit in uw leven de morgen ontboden, De dageraad zijn plaats bestemd,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
Om de zomen der aarde te bezetten En er vlammen uit te schudden?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Zij flonkert als een kostbare zegelsteen, Wordt bontgeverfd als een kleed,
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
Totdat de stralen hun licht wordt ontnomen, Hun opgeheven arm wordt gebroken.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Zijt ge doorgedrongen tot de bronnen der zee, Hebt ge de bodem van de Oceaan bewandeld;
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Zijn u de poorten des doods getoond, De wachters der duisternis u verschenen;
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Hebt ge de breedten der aarde omvat: Zeg op, wanneer ge dit allemaal weet!
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Waar is de weg naar de woning van het licht, En waar heeft de duisternis haar verblijf,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
Zodat gij ze naar hun plaats kunt brengen, En hun de paden naar huis kunt leren?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Ge weet het toch, want toen werdt ge geboren, Het getal van uw jaren is immers zo groot!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Zijt ge doorgedrongen tot de schuren der sneeuw, Hebt ge de opslagplaatsen van de hagel aanschouwd,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Die Ik heb opgespaard voor de tijd van benauwing, Voor de dag van aanval en strijd?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Waar is de weg, waar de kou zich verspreidt, Waar de oostenwind over de aarde giert?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Wie heeft voor de stortvloed kanalen gegraven, En paden voor de donderwolken,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
Om regen te geven op onbewoond land, Op steppen, waar zich geen mens bevindt;
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
Om woestijn en wildernis te verzadigen, Uit de dorre grond het gras te doen spruiten?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Heeft de regen een vader, Of wie heeft de druppels van de dauw verwekt;
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Uit wiens schoot is het ijs te voorschijn gekomen, Wie heeft het rijp in de lucht gebaard?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
De wateren worden hard als steen, De vlakte van de Afgrond sluit zich aaneen!
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Kunt gij de banden der Plejaden knopen, Of de boeien van de Orion slaken;
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Kunt gij de maan op tijd naar buiten doen treden, Leidt gij de Beer met zijn jongen?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Schrijft gij de hemel de wetten voor, Stelt gij zijn macht over de aarde vast;
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Verheft gij uw stem tot de wolken, Gehoorzaamt ù de watervloed?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Zendt gij de bliksems uit, en ze gaan; Zeggen ze tot u: Hier zijn we terug?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Wie heeft inzicht aan den reiger gegeven Verstand geschonken aan den haan;
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Wie telt met wijsheid de wolken af, En giet de zakken van de hemel leeg:
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
Wanneer de bodem hard is als ijzer, De kluiten aan elkander kleven?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Jaagt gij een prooi voor de leeuwin, Stilt gij de honger der welpen,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
Wanneer ze in hun holen liggen, Of loeren tussen de struiken?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Wie geeft ze tegen de avond haar buit, Wanneer haar jongen tot de Godheid roepen, En zonder voedsel rond blijven snuffelen, Op zoek naar spijs?

< Yobu 38 >