< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Derefter svarede Herren Job ud af Stormen og sagde:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Hvo er den, som formørker Guds Raad med Tale uden Forstand.
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Bind op om dine Lænder som en Mand, saa vil jeg spørge dig, og undervis du mig!
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Hvor var du, der jeg grundfæstede Jorden? forkynd det, hvis du har Indsigt?
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Hvo har sat dens Maal? du ved det vel? eller hvo udstrakte Snoren over den?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
Hvorpaa ere dens Piller nedsænkede? eller hvo har lagt dens Hjørnesten?
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
der Morgenstjerner sang til Hobe, og alle Guds Børn raabte af Glæde.
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Og hvo lukkede for Havet med Døre, der det brød frem, gik ud af Moders Liv,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
der jeg gjorde Sky til dets Klædning og Mørke til dets Svøb,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
der jeg afstak for det min Grænse og satte Stang og Døre for det
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
og sagde: Hertil skal du komme og ikke længere; og her skal være sat Grænse for dine stolte Bølger?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Har du i dine Dage givet Befaling til Morgenen? har du vist Morgenrøden dens Sted,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
til at gribe Jorden ved dens Flige, saa at de ugudelige rystes bort fra den?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
saa denne forvandler sig som Leret, hvori Seglet trykkes, og Tingene fremstille sig som i deres Klædebon,
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
og de ugudelige unddrages deres Lys, og den opløftede Arm sønderbrydes?
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Er du kommen til Havets Kilder? og har du vandret paa Dybets Bund?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Have Dødens Porte opladt sig for dig? eller saa du Dødens Skygges Porte?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Har du overskuet Jordens Bredde? forkynd det, dersom du kender det alt sammen!
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Hvor er Vejen did, hvor Lyset mon bo, og hvor er Mørkets Sted,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
at du kunde bringe det til dets Landemærke, og at du kendte Stierne til dets Hus?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Du ved det; thi den Gang blev du jo født, og dine Dages Tal er stort!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Er du kommen til Forraadskamrene for Sneen, eller saa du Forraadskamrene for Hagelen,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
hvilke jeg har sparet til Trængsels Tid, til Strids og Krigs Dag.
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Hvor er den Vej, hvor Lyset deler sig, hvor Østenvejret spreder sig over Jorden?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Hvo brød Render til Vandskyl og Vej til Lynet, som gaar foran Torden,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
for at lade regne paa det Land, hvor ingen er, i Ørken, hvor intet Menneske er,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
for at mætte de øde og ødelagte Steder og bringe Græsbunden til at spire?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Har Regnen vel en Fader? eller hvo har avlet Duggens Draaber?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
Af hvis Moderliv er Frost udgangen? og hvo fødte Rimfrost under Himmelen?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Vandet skjuler sig, som var det en Sten, og Dybets Overflade slutter sig sammen.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Kan du knytte Syvstjernens Baand, eller løse Orions Reb?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Kan du lade Dyrekredsens Stjerner komme frem til deres Tid? eller føre Bjørnen med dens Unger frem?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Kender du Himmelens Love? eller kan du bestemme dens Herredømme over Jorden?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Kan du opløfte din Røst til Skyen, at Vands Mangfoldighed maa skjule dig?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Kan du udlade Lynene, at de fare frem, og at de sige til dig: Se, her ere vi?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Hvo lagde Visdom i Hjertets Inderste? eller hvo gav Forstand i Tanken?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Hvo kan tælle Skyerne med Visdom? og hvo kan udgyde Himmelens Vandbeholdere,
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
idet Støv løber sammen til en Støbning, og Jordklumperne hænge ved hverandre?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Kan du jage Rov til Løvinden og fylde de unge Løvers Graadighed,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
naar de lægge sig ned i deres Boliger og blive i Skjul for at lure?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Hvo skaffer Ravnen dens Føde, naar dens Unger skrige til Gud, naar de fare hid og did, fordi de intet have at æde?

< Yobu 38 >