< Yobu 38 >

1 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
Тогава Господ отговори на Иова из бурята и каза:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
Кой е тогава този, който помрачава Моя съвет С неразумни думи?
3 Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
Опаши сега кръста си като мъж, И ще те попитам; и ти ми изяснявай,
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
Где беше ти, когато основах земята? Извести, ако си разумен:
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
Кой определи мерките й? (ако знаеш) Или кой тегли връв за мерене по нея?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
На какво се вдълбочиха основите й? Или кой положи краеъгълния й камък,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
Когато звездите на зората пееха заедно, И всички Божии синове възклицаваха от радост?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
Или кой затвори морето с врати, Когато се устреми та излезе из матка,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
Когато го облякох с облак И го пових с мъгла,
10 pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
И поставих му граница от Мене, Турих лостове и врати,
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
И рекох: До тук ще дохождаш, но не по-нататък, И тук ще се спират гордите ти вълни?
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
Откак започнаха дните ти заповядал ли си ти на утрото И показал на зората мястото й,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
За да обхване краищата на земята, Така щото да се изтърсят от нея злодейците
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
Та да се преобразува тя, както глина под печат, И всичко да изпъква като че ли в облекло,
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
А от нечестивите да се отнеме виделината им, И издигнатата им мишца да се строши?
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
Проникнал ли си до изворите на морето? Или ходил ли си да изследваш бездната?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
Откриха ли се на тебе вратите на смъртта? Или видял ли си сенчестите врати на смъртта?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
Схванал ли си широчината на земята? Кажи, ако си разбрал всичко това.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
Где е пътят към обиталището на светлината? И на тъмнината где е мястото й,
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
За да й заведеш до границата й, И да познаеш пътеките към дома й?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
Без съмнение, ти знаеш, защото тогаз си се родил, И голямо е числото на твоите дни!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
Влизал ли си в съкровищниците за снега, Или виждал ли си съкровищниците за градушката,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
Които пазя за време на скръб, За ден на бой и на война?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
Що е пътят за мястото, гдето се разсява светлината, Или се разпръсва по земята източният вятър?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
Кой е разцепил водопровод за проливните дъждове, Или път за светкавицата на гръма,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
За да се докара дъжд върху ненаселена земя, Върху пустинята, гдето няма човек,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
За да насити пустата и запустяла земя. И да направи нежната трева да изникне?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
Дъждът има ли баща? Или кой е родил капките на росата?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
От чия матка излиза ледът? И кой е родил небесната слана?
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
Когато водите се втвърдяват като камък, И повърхността на бездната се смръзва.
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
Ти ли връзваш връзките на Плеадите, Или развързваш въжетата на Ориона?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
Извеждаш ли Мазарот на времето му? Или управляваш ли Мечката с малките й?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
Познаваш ли законите на небето? Установяваш ли неговото владичество върху земята?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
Издигаш ли гласа си до облаците, За да те покрият изобилни води?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
Изпращаш ли светкавици, та да излизат И да ти казват: Ето ни?
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
Кой е турил мъдрост в облаците? Или кой е дал разум на гъстите облаци?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
Кой с мъдрост брои облаците? Или кой излива небесните мехове
38 pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
Та да се сгъстява пръстта в куп, И буците да се слепят?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
Улавят ли лов за лъвицата? Или насищат ли охотата на лъвовите малки,
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
Когато седят в рововете си, И остават в скривалищата за да причакват?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
Кой приготвя за враната храната й, Когато пилетата й от нямане храна Се скитат и викат към Бога?

< Yobu 38 >