< Yobu 37 >

1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
Tudi ob tem moje srce trepeta in je premaknjeno iz svojega mesta.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Pozorno prisluhnite hrupu njegovega glasu in zvoku, ki gre iz njegovih ust.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
Tega usmerja pod celotnim nebom in svoje bliskanje do koncev zemlje.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
Za tem rjovi glas. Grmi z glasom svoje odličnosti in ne bo jih zadržal, ko se zasliši njegov glas.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
Bog s svojim glasom čudovito grmi. Dela velike stvari, ki jih ne moremo doumeti.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Kajti snegu pravi: ›Bodi na zemlji, ‹ podobno majhnemu dežju in velikemu dežju njegove moči.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Pečati roko vsakega človeka, da bi vsi ljudje lahko poznali njegovo delo.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Potem gredo živali v brloge in ostanejo na svojih mestih.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
Iz juga prihaja vrtinčast veter in mraz iz severa.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
Z dihom Boga je dana zmrzal in širina vodá je omejena.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Tudi z namakanjem obtežuje debel oblak. Razpršuje svoj svetli oblak.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
Ta je obrnjen ob njegovih nasvetih, da lahko naredijo karkoli jim zapoveduje na obličju zemeljskega [kroga] na zemlji.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
Povzroča mu, da pride, bodisi za grajanje ali za njegovo deželo ali za usmiljenje.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Prisluhni temu, oh Job. Stoj mirno in preudari čudovita Božja dela.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Ali veš, kdaj jih je Bog razporedil in svetlobi svojega oblaka velel, da zasije?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Mar poznaš izravnavanja oblakov, čudovita dela njega, ki je popoln v spoznanju?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
Kako so tvoje obleke tople, ko z južnim vetrom umiri zemljo?
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
Ali si ti z njim razprostrl nebo, ki je močno in kakor staljeno zrcalo?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Pouči nas, kaj mu bomo rekli, kajti svojega govora ne moremo urediti zaradi teme.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Mar mu bo povedano, da jaz govorim? Če človek govori, bo zagotovo požrt.
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
Sedaj ljudje ne vidimo svetle svetlobe, ki je v oblakih, toda veter gre mimo in jih očisti.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Lepo vreme prihaja iz severa. Z Bogom je strašno veličanstvo.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
Glede Vsemogočnega, ne moremo ga srečati. Odličen je v moči, v sodbi in v obilici pravice. Ne bo prizadel.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Ljudje se ga zato bojijo. Ne ozira se na nobenega od tistih, ki so modrega srca.«

< Yobu 37 >