< Yobu 37 >
1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
Mpo na yango, motema na ngai ezali kolenga mpe ezali kobeta makasi lokola nde elingi kobima na esika na yango.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Yoka! Yoka makelele ya mongongo na Ye, makelele oyo ezali kobima na monoko na Ye.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
Azali kotinda yango na mokili mobimba, mpe kake na Ye kino na suka ya mokili.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
Sima na yango, konguluma na Ye ekoyokana, akoganga makasi na mongongo ya bokonzi na Ye; akokanga mikalikali ya monoko na Ye te, wana mongongo na Ye ezali koyokana.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
Na nzela ya mongongo na Ye ya makasi, Nzambe asalaka bikamwa, asalaka makambo minene, makambo minene oyo mayele na biso ekoki kososola te.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Alobaka na mvula ya pembe: ‹ Sopana na mabele. › Alobaka bongo lisusu na mvula ya makasi: ‹ Sopana. ›
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Boye, atiaka kashe na loboko ya moto nyonso mpo ete moto nyonso ayeba misala na Ye. Atondisaka bato nyonso na somo ya nguya na Ye.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Banyama ezongaka na bandako na yango mpe evandaka kati na libulu na yango.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
Mopepe makasi ewutaka na ngambo ya sude, malili mpe mipepe, na ngambo ya nor.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
Na mopepe oyo ebimaka na monoko ya Nzambe, mayi ebongwanaka libanga mpe bitima ya mayi ekondaka.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Atondisaka mapata na mayi, mpe pole na Ye epanzaka mapata ya mvula.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
Na makasi na Ye, mapata ebalukaka na bangambo nyonso mpo na kokokisa nyonso oyo Ye atindaka yango kosala kati na mokili.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
Ezalaka mpo na kopesa etumbu na mokili to mpo na kopambola yango.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Yoka, Yobo! Telema mpe sosola bikamwa ya Nzambe.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Oyebi ndenge nini Nzambe akambaka mapata, mpe ndenge nini angengisaka mikalikali na Ye na mapata?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Oyebi ndenge nini mapata evandaka malamu? Ezali bikamwa ya Ye-Oyo-Akoka-Na-Boyebi-Nyonso.
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
Bilamba na yo ezali na moto, nzokande mabele ezali konyokwama na mopepe ya midi.
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
Boni, okoki solo kosunga Nzambe mpo na kotanda likolo elongo na Ye, likolo oyo ezali makasi lokola talatala ya ebende banyangwisa na moto?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Yebisa biso makambo oyo tosengeli koloba na Ye; tokoki koloba likambo moko te mpo na molili na biso.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Boni, basengeli koyebisa Ye ete nalingi koloba? Basengeli koyebisa Ye mpo ete ayeba yango?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
Na pwasa, moto moko te azali komona lisusu pole; ebombami kati na mapata. Kasi soki mopepe eleki, elongoli yango nyonso.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Kongenga lokola wolo ezali koya wuta na ngambo ya nor. Nzambe avandi kati na nkembo ya somo.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
Azali Nkolo-Na-Nguya-Nyonso, tokoki te kokoma esika Ye azali; azali monene na nguya mpe na solo; azali Mokonzi ya sembo, akoki konyokola te moto oyo azali sembo.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Yango wana bato basengeli kokumisa Ye, kasi Ye atiaka miso na Ye te likolo ya bato oyo bakanisaka ete bazali bato ya bwanya. »