< Yobu 37 >
1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
これがためにわが心もまたわななき、その所からとび離れる。
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
聞け、神の声のとどろきを、またその口から出るささやきを。
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
彼はこれを天が下に放ち、その光を地のすみずみまで至らせられる。
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
その後、声とどろき、彼はそのいかめしい声をもって鳴り渡られる。その声の聞える時、彼はいなずまを引きとめられない。
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
神はその驚くべき声をもって鳴り渡り、われわれの悟りえない大いなる事を行われる。
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
彼は雪に向かって『地に降れ』と命じ、夕立ちおよび雨に向かって『強く降れ』と命じられる。
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
彼はすべての人の手を封じられる。これはすべての人にみわざを知らせるためである。
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
その時、獣は穴に入り、そのほらにとどまる。
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
つむじ風はそのへやから、寒さは北風から来る。
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
神のいぶきによって氷が張り、広々とした水は凍る。
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
彼は濃い雲に水気を負わせ、雲はそのいなずまを散らす。
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
これは彼の導きによってめぐる。彼の命じるところをことごとく世界のおもてに行うためである。
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
神がこれらをこさせるのは、懲しめのため、あるいはその地のため、あるいはいつくしみのためである。
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
ヨブよ、これを聞け、立って神のくすしきみわざを考えよ。
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
あなたは知っているか、神がいかにこれらに命じて、その雲の光を輝かされるかを。
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
あなたは知っているか、雲のつりあいと、知識の全き者のくすしきみわざを。
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
南風によって地が穏やかになる時、あなたの着物が熱くなることを。
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
あなたは鋳た鏡のように堅い大空を、彼のように張ることができるか。
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
われわれが彼に言うべき事をわれわれに教えよ、われわれは暗くて、言葉をつらねることはできない。
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
わたしは語ることがあると彼に告げることができようか、人は滅ぼされることを望むであろうか。
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
光が空に輝いているとき、風過ぎて空を清めると、人々はその光を見ることができない。
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
北から黄金のような輝きがでてくる。神には恐るべき威光がある。
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
全能者はわれわれはこれを見いだすことができない。彼は力と公義とにすぐれ、正義に満ちて、これを曲げることはない。
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
それゆえ、人々は彼を恐れる。彼はみずから賢いと思う者を顧みられない」。