< Yobu 37 >
1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
“Also, my heart trembles at this, And it moves from its place.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Listen diligently to the trembling of His voice, Indeed, the sound goes forth from His mouth.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
He directs it under the whole heavens, And its light [is] over the skirts of the earth.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
A voice roars after it—He thunders with the voice of His excellence, And He does not hold them back, When His voice is heard.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
God thunders with His voice wonderfully, Doing great things and we do not know.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
For He says to snow: Be [on] the earth. And the small rain and great rain of His power.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Into the hand of every man he seals, For the knowledge by all men of His work.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
And the beast enters into [its] lair, And it continues in its habitations.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
From the inner chamber comes a windstorm, And from scatterings winds—cold,
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
From the breath of God is frost given, And the breadth of waters is constricted,
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Indeed, by filling He presses out a cloud, [and] His light scatters a cloud.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
And it is turning itself around by His counsels, For their doing all He commands them, On the face of the habitable earth.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
Whether for a rod, or for His land, Or for kindness—He causes it to come.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Hear this, O Job, Stand and consider the wonders of God.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Do you know when God places them, And caused the light of His cloud to shine?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Do you know the balancings of a cloud? The wonders of the Perfect in knowledge?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
How your garments [are] warm, In the quieting of the earth from the south?
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
You have made an expanse with Him For the clouds—strong as a hard mirror!
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Let us know what we say to Him, We do not set in array because of darkness.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Is it declared to Him that I speak? If a man has spoken, surely he is swallowed up.
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
And now, they have not seen the light, It [is] bright in the clouds, And the wind has passed by and cleanses them.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
It comes from the golden north, Fearful splendor [is] beside God.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
The Mighty! We have not found Him out, High in power and judgment, He does not answer! And abundant in righteousness,
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Therefore men fear Him, He does not see any of the wise of heart.”