< Yobu 37 >
1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
At this also my heart trembleth, and is moved out of its place.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Hear attentively the noise of His voice, and the sound that goeth out of His mouth.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
He sendeth it forth under the whole heaven, and His lightning unto the ends of the earth.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
After it a voice roareth; He thundereth with the voice of His majesty; and He stayeth them not when His voice is heard.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
God thundereth marvellously with His voice; great things doeth He, which we cannot comprehend.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
For He saith to the snow: 'Fall thou on the earth'; likewise to the shower of rain, and to the showers of His mighty rain.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
He sealeth up the hand of every man, that all men whom He hath made may know it.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Then the beasts go into coverts, and remain in their dens.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
Out of the Chamber cometh the storm; and cold out of the north.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
By the breath of God ice is given, and the breadth of the waters is straitened.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Yea, He ladeth the thick cloud with moister, He spreadeth abroad the cloud of His lightning;
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
And they are turned round about by His guidance, that they may do whatsoever He commandeth them upon the face of the habitable world:
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
Whether it be for correction, or for His earth, or for mercy, that He cause it to come.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Hearken unto this, O Job; stand still, and consider the wondrous works of God.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Dost thou know how God enjoineth them, and causeth the lightning of His cloud to shine?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Dost thou know the balancings of the clouds, the wondrous works of Him who is perfect in knowledge?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
Thou whose garments are warm, when the earth is still by reason of the south wind;
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
Canst thou with Him spread out the sky, which is strong as a molten mirror?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Teach us what we shall say unto Him; for we cannot order our speech by reason of darkness.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Shall it be told Him that I would speak? Or should a man wish that he were swallowed up?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
And now men see not the light which is bright in the skies; but the wind passeth, and cleanseth them.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Out of the north cometh golden splendour, about God is terrible majesty.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
The Almighty, whom we cannot find out, is excellent in power, yet to judgment and plenteous justice He doeth no violence.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Men do therefore fear Him; He regardeth not any that are wise of heart.