< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
І далі Елігу казав:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
„Почекай мені тро́хи, й тобі покажу́, бо ще́ є про Бога слова́.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Зачну́ виклада́ти я зда́лека, і Творце́ві своєму віддам справедливість.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Бо справді слова́ мої не неправдиві, — я з тобою безва́дний в знанні́.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Таж Бог си́льний, і не відкидає ніко́го, Він міцни́й в силі серця.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Не лишає безбожного Він при житті, але право для бідних дає.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Від праведного Він очей Своїх не відверта́є, але їх садо́вить з царями на троні наза́вжди, — і вони підвищаються.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
А як тільки вони ланцюга́ми пов'я́зані, і тримаються в пу́тах біди́,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
то Він їм представляє їх вчинок та їхні провини, що багато їх стало.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
Відкриває Він ухо їх для осторо́ги, та вели́ть, щоб вернулися від беззако́ння.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Якщо тільки послу́хаються, та стануть служити Йому, покі́нчать вони свої дні у добрі, а ро́ки свої у приє́мнощах.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Коли ж не послухаються, то наскочать на ра́тище, і покі́нчать життя без знання́.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
А злосерді кладуть гнів на себе, не кричать, коли в'яже Він їх.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
У мо́лодості помирає душа їх, а їхня живая — поміж блудника́ми.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Він визволяє убогого з горя його, а в переслі́дуванні відкриває їм ухо.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Також і тебе Він би ви́бавив був із тісноти́ на широ́кість, що в ній нема у́тиску, а те, що на стіл твій поклалося б, повне то́вщу було б.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Та правом безбожного ти перепо́внений, право ж та суд підпира́ють люди́ну.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Отож лютість нехай не намо́вить тебе до плеска́ння в долоні, а о́куп великий нехай не заве́рне з дороги тебе.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Чи в біді допоможе твій зойк та всі змі́цнення сили?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Не квапся до ночі тієї, коли ви́рвані будуть народи із місця свого́.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Стережись, не звертайся до зла, яке за́мість біди ти обрав.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Отож, Бог найвищий у силі Своїй, — хто навчає, як Він?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Хто дорогу Його Йому вказувати бу́де? І хто скаже: „Ти кривду зробив?“
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Пам'ятай, щоб звели́чувати Його вчинок, про якого виспівують люди,
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
що його бачить всяка люди́на, чоловік приглядається зда́лека.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Отож, Бог великий та недовідо́мий, і недосліди́ме число Його літ!
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Бо стягає Він краплі води, і доще́м вони падають з хмари Його,
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
що хмари спускають його, і спада́ють дощем на багато людей.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Також хто зрозуміє розтя́гнення хмари, грім намету Його?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Отож, розтягає Він світло Своє над Собою і мо́рську глибі́нь закриває,
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
бо ними Він судить наро́ди, багато поживи дає.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Він тримає в руках Своїх бли́скавку, і керує її проти цілі.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Її гу́ркіт звіщає про неї, і при́хід її відчуває й худо́ба.

< Yobu 36 >