< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Још говори Елијуј и рече:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Потрпи ме мало, и показаћу ти, јер још има шта бих говорио за Бога.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Почећу издалека беседу своју, и показаћу да је Творац мој праведан.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Доиста, неће бити лажне речи моје, код тебе је који право мисли.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Гле, Бог је силан, али никога не одбацује, силан је снагом срчаном.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Не да живети безбожнику, а невољницима чини правду.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Не одвраћа од праведника очију својих, него још с царевима на престо посађује их на век, те се узвишују.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Ако ли су оковани у пута и свезани ужима невољничким,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
Тада им напомиње дела њихова и безакоња њихова како су силна.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
И отвара Му ухо да би се поправили, и говори им да се врате од безакоња.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Ако послушају и стану им служити, довршују дане своје у добру и године своје у радости.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Ако ли не послушају, гину од мача и умиру с безумља.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
А који су лицемерног срца, навлаче гнев и не вичу кад их повеже;
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Умире у младости душа њихова и живот њихов међу курвама.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Избавља невољника из невоље његове и отвара му ухо у муци.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Тако би и тебе извео из тескобе на пространо место, где ништа не досађује, и мирни сто твој био би пун претилине.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Али си заслужио суд безбожнички; и суд и правда снађе те.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Доиста, гнев је на теби; гледај да те не одбаци у карању, те те велики откуп неће избавити.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Хоће ли гледати на твоје богатство? Неће ни на злато ни на какву силу блага твог.
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Не уздиши за ноћу у коју народи одлазе на своје место.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Чувај се да не погледаш на таштину и волиш на њу него невољу.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Гле, Бог је највиши својом силом, ко је учитељ као Он?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Ко Му је одредио пут Његов? Или ко ће Му рећи: Чиниш неправо?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Опомињи се да величаш дела Његова, која гледају људи.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Сви људи виде их, сваки их гледа из далека.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Гле, Бог је велик, и не можемо Га познати, број година Његових не може се докучити.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Јер Он стеже капље водене, које лију дажд из облака Његових;
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
Кад теку облаци, капљу на мноштво људско.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
И ко би разумео простор облацима и грмљаву у шатору његовом?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Како простире над њим светлост своју, и дубине морске покрива?
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Тиме суди народима, даје хране изобила.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Рукама заклања светлост, и наређује кога да срете,
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Јављајући према њему добру вољу своју, и према стоци и према роду земаљском.

< Yobu 36 >