< Yobu 36 >
1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Prosseguiu Eliú ainda, dizendo:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Espera-me um pouco, e eu te mostrarei que ainda há palavras a favor de Deus.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Desde longe trarei meu conhecimento, e a meu Criador atribuirei a justiça.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Porque verdadeiramente minhas palavras não serão falsas; contigo está um que tem completo conhecimento.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Eis que Deus é grande, porém despreza ninguém; grande ele é em poder de entendimento.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Ele não permite o perverso viver, e faz justiça aos aflitos.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Ele não tira seus olhos do justo; ao contrário, ele os faz sentar com os reis no trono, e [assim] são exaltados.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
E se estiverem presos em grilhões, e detidos com cordas de aflição,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
Então ele lhes faz saber as obras que fizeram, e suas transgressões, das quais se orgulharam.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
E revela a seus ouvidos, para que sejam disciplinados; e lhes diz, para que se convertam da maldade.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Se ouvirem, e [o] servirem, acabarão seus dias em prosperidade, e seus anos em prazeres.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Porém se não ouvirem, perecerão pela espada, e morrerão sem conhecimento.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
E os hipócritas de coração acumulam a ira [divina]; e quando ele os amarrar, mesmo assim não clamam.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
A alma deles morrerá em sua juventude, e sua vida entre os pervertidos.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Ele livra o aflito de sua aflição, e na opressão ele revela a seus ouvidos.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Assim também ele pode te desviar da boca da angústia [para] um lugar amplo, onde não haveria aperto; para o conforto de tua mesa, cheia dos melhores alimentos.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Mas tu estás cheio do julgamento do perverso; o julgamento e a justiça te tomam.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Por causa da furor, [guarda-te] para que não sejas seduzido pela riqueza, nem que um grande suborno te faça desviar.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Pode, por acaso, a tua riqueza te sustentar para que não tenhas aflição, mesmo com todos os esforços de [teu] poder?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Não anseies pela noite, em que os povos são tomados de seu lugar.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Guarda-te, e não te voltes para a maldade; pois por isto que tens sido testado com miséria.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Eis que Deus é exaltado em seu poder; que instrutor há como ele?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Quem lhe indica o seu caminho? Quem poderá lhe dizer: Cometeste maldade?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Lembra-te de engrandeceres sua obra, a qual os seres humanos contemplam.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Todas as pessoas a veem; o ser humano a enxerga de longe.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Eis que Deus é grande, e nós não o compreendemos; não se pode descobrir o número de seus anos.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Ele traz para cima as gotas das águas, que derramam a chuva de seu vapor;
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
A qual as nuvens destilam, gotejando abundantemente sobre o ser humano.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Poderá alguém entender a extensão das nuvens, [e] os estrondos de seu pavilhão?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Eis que estende sobre ele sua luz, e cobre as profundezas do mar.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Pois por estas coisas ele julga aos povos, e dá alimento em abundância.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Ele cobre as mãos com o relâmpago, e dá ordens para que atinja o alvo.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
O trovão anuncia sua presença; o gado também [prenuncia a tempestade] que se aproxima.