< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
U-Elihu waqhubeka esithi:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
“Ake lingibekezelele okwesikhatshana ukuze ngilitshengise ukuthi kunengi okumele kutshiwo ngobuhle bukaNkulunkulu.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Ngiluzuza kude ulwazi lwami; ngithi ukwahlulela okulungileyo ngokukaMenzi wami.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Yiba leqiniso ukuthi amazwi ami aqinisile; yena opheleleyo elwazini ulawe.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
UNkulunkulu ulamandla, kodwa keyisi muntu; ulamandla njalo katshedi ezimisweni zakhe.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Ababi kabayekeli bephila kodwa abahluphekayo uyabapha okubafaneleyo.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Kawasusi amehlo akhe kwabalungileyo; ubakhweza esihlalweni kanye lamakhosi abaphakamise nini lanini.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Kodwa nxa abantu bebotshwe ngamaketane, bethiwe nko ngezibopho zezinhlupheko,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
uyabatshela lokho abakwenzileyo, ukuthi benze isono ngokuziphakamisa.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
Ubenza balalele ukuqondiswa abalaye ukuthi baphenduke ebubini babo.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Nxa bemlalela bamkhonze, zonke insuku zabo eziseleyo zizaphumelela, leminyaka yabo ibe ngeyokusuthiseka.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Kodwa nxa bengalaleli, bazabhubha ngenkemba, bafe bengelalwazi.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
Abangamesabiyo uNkulunkulu bagodle ukusola enhliziyweni; loba angaze ababophe kabaceli ukusizwa.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Bafa besesebatsha, bephakathi kweziphingi ezingamadoda, ezihlala ezindaweni zokukhonzela.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Kodwa labo abahluphekayo uyabakhulula ekuhluphekeni kwabo; ukhuluma labo besezinkathazweni zabo.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Uyakulimukisa ukuthi uphume emihlathini yosizi uye endaweni ebanzi, ekhululekileyo njalo engelazibopho, ebumnandini betafula yakho igcwele izidlo ezimnandi.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Kodwa manje usindwa yikwahlulelwa okulungele ababi; ukuthonisiswa lokwahlulelwa ngokulunga yikho osekukuduba.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Qaphela kungabikhona okulingayo ngenotho; ungavumeli ukuthengwa ngemali kukususe endleleni.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Kambe inotho yakho loba konke ukutshikatshika kwakho kungakusekela ukuze ungangeni osizini na?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Ungalangazeleli ubusuku, ukuze uyohudula abantu ezindaweni zabo.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Qaphela ungangeni kokubi, okukhanya ingathi uyakuthanda kulokuhlupheka.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
UNkulunkulu uphakeme ngamandla akhe. Ngubani ongafundisa njengaye na?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Ngubani omisele izindlela zakhe na, loba othe kuye, ‘Usuwenze okungalunganga?’
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Khumbula ukukhulisa umsebenzi wakhe, abantu abawudumisileyo ngengoma.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Bonke abantu jikelele bakubonile lokhu; abantu bakukhangela bemi khatshana.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Ubukhulu bukaNkulunkulu bungaphezulu kokuzwisisa kwethu! Iminyaka yakhe ingezake yaziwe.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Uyawadonsa amathonsi amanzi, aqulungane abe lizulu elingena ezifuleni;
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
amayezi athulula amanzi awo kune izulu elikhulu ebantwini.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Ngubani ongakuzwisisa ukuthi uwendlala njani amayezi na, ukuthi ukhwaza njani esesiqongweni sakhe na?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Ake libone ukuthi uwuhlakaza njani umbane wakhe azizingelezele ngawo, abhukutshe ezinzikini zolwandle.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Yiyo indlela abusa ngayo izizwe aziphe ukudla okunengi.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Ugcwalisa izandla zakhe ngombane awukhombise lapho omele utshaye khona.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Ukuduma kwakhe kubika isiphepho esizayo; lenkomo ziyatshengisa ukuza kwaso.”

< Yobu 36 >