< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Eriku ne yeeyongera okwogera nti,
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
“Yongera okuŋŋumiikirizaako katono nkulage, nkyalina bye nnina okwogera ebifa ku Katonda.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Amagezi ge nnina gava wala, era mmanyi nga Omutonzi wange alamula mu bwenkanya.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Eky’amazima ebigambo byange si bikyamu, oyo akakasa by’amanyi y’ayogera naawe.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
“Laba, Katonda wa buyinza, tanyooma bantu; w’amaanyi, anywerera ku bigendererwa bye.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Talamya bakozi ba bibi, era awa ababonyaabonyezebwa ebibasaanira.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Taggya maaso ge ku batuukirivu, abatuuza ku ntebe ey’obwakabaka n’abagulumiza emirembe n’emirembe.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Naye abantu bwe baba basibiddwa enjegere nga banywezeddwa n’emiguwa egy’okulumwa
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
n’abategeeza ensobi zaabwe, n’okwonoona kwabwe, nti, beewaggudde,
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
aggula amatu gaabwe bawulirize okunenyezebwa n’abalagira beenenye ekibi kyabwe.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Bwe bamugondera ne bamuweereza, ennaku zaabwe zonna balizimala mu kwesiima, era n’emyaka gyabwe mu kusanyuka.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Naye bwe batamugondera, baalizikirizibwa n’ekitala, bafe nga tebalina magezi.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
“Ab’emitima egitatya Katonda baba n’obukyayi. Ne bw’abasiba, tebamukaabirira abasumulule.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Bafiira mu buvubuka bwabwe era obulamu bwabwe buzikiririra mu basajja abenzi.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Anunula anyigirizibwa mu kubonaabona kwe, n’aggula okutu kwe mu kujoogebwa kwe.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
“Akusendasenda okukuggya mu kamwa k’okubonaabona, akuteeke mu kifo ekigazi ekitaliimu kuziyizibwa, omanye emirembe gy’emeeza yo ejjudde emmere ennungi.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Naye kaakano weetisse omugugu ogw’okusalirwa omusango abakozi b’ebibi gwe basaanira; okusalirwa omusango n’obwenkanya byakunyweza.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Weegendereze oleme kukkiriza kusendebwasendebwa; obunene bw’enguzi buleme okukukyamya.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Obugagga bwo oba okufuba kwo kwonna binaakuyamba okukuggya mu buyinike?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Teweegomba budde bwa kiro olyoke owalule abantu okuva mu bifo byabwe.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Weegendereze oleme kukola bitali bya butuukirivu, by’osinga okwagala okukira okubonyaabonyezebwa.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
“Laba Katonda yagulumira mu maanyi ge; ani ayigiriza nga ye?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Ani eyali amukubidde amakubo, oba okumugamba nti, ‘Ky’okoze si kituufu?’
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Jjukira ng’oteekwa okugulumizanga emirimu gye, abantu gye bayimba mu nnyimba.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Abantu bonna baagiraba, omuntu agirengerera wala.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Laba, Katonda agulumizibwe! Assukiridde okutegeera kwaffe; obungi bw’emyaka gye tebunoonyezeka.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
“Kubanga akuŋŋaanya amatondo g’amazzi, agafuuka enkuba etonnya mu bugga;
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
ebire bivaamu amazzi gaabyo, enkuba n’ekuba abantu.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Ani ayinza okutegeera engeri gy’asaasaanyamu ebire, okubwatuka okuva ku kituuti kye?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Laba, asaasaanya okumyansa kw’eggulu, era n’abikka obuziba bw’ennyanja.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Eyo y’engeri gy’afugamu amawanga, n’agawa emmere mu bungi.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Emikono gye agijjuza eraddu, n’agiragira ekube ebifo bye yeerondeddemu.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Okubwatuka kwayo kulangirira kibuyaga ajja, n’ente ne zirangirira okujja kwayo.”

< Yobu 36 >