< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Addens quoque Eliu, hæc locutus est:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Sustine me paululum, et indicabo tibi: adhuc enim habeo quod pro Deo loquar.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Repetam scientiam meam a principio, et operatorem meum probabo justum.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Vere enim absque mendacio sermones mei, et perfecta scientia probabitur tibi.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Deus potentes non abjicit, cum et ipse sit potens:
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
sed non salvat impios, et judicium pauperibus tribuit.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Non auferet a justo oculos suos: et reges in solio collocat in perpetuum, et illi eriguntur.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Et si fuerint in catenis, et vinciantur funibus paupertatis,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
indicabit eis opera eorum, et scelera eorum, quia violenti fuerunt.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
Revelabit quoque aurem eorum, ut corripiat: et loquetur, ut revertantur ab iniquitate.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Si audierint et observaverint, complebunt dies suos in bono, et annos suos in gloria:
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
si autem non audierint, transibunt per gladium, et consumentur in stultitia.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
Simulatores et callidi provocant iram Dei, neque clamabunt cum vincti fuerint.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Morietur in tempestate anima eorum, et vita eorum inter effeminatos.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Eripiet de angustia sua pauperem, et revelabit in tribulatione aurem ejus.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Igitur salvabit te de ore angusto latissime, et non habente fundamentum subter se: requies autem mensæ tuæ erit plena pinguedine.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Causa tua quasi impii judicata est: causam judiciumque recipies.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Non te ergo superet ira ut aliquem opprimas: nec multitudo donorum inclinet te.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Depone magnitudinem tuam absque tribulatione, et omnes robustos fortitudine.
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Ne protrahas noctem, ut ascendant populi pro eis.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Cave ne declines ad iniquitatem: hanc enim cœpisti sequi post miseriam.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Ecce Deus excelsus in fortitudine sua, et nullus ei similis in legislatoribus.
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Quis poterit scrutari vias ejus? aut quis potest ei dicere: Operatus es iniquitatem?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Memento quod ignores opus ejus, de quo cecinerunt viri.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Omnes homines vident eum: unusquisque intuetur procul.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Ecce Deus magnus vincens scientiam nostram: numerus annorum ejus inæstimabilis.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Qui aufert stillas pluviæ, et effundit imbres ad instar gurgitum,
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
qui de nubibus fluunt quæ prætexunt cuncta desuper.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Si voluerit extendere nubes quasi tentorium suum,
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
et fulgurare lumine suo desuper, cardines quoque maris operiet.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Per hæc enim judicat populos, et dat escas multis mortalibus.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
In manibus abscondit lucem, et præcepit ei ut rursus adveniat.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Annuntiat de ea amico suo, quod possessio ejus sit, et ad eam possit ascendere.

< Yobu 36 >