< Yobu 36 >
1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Eliu continuò a dire:
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Abbi un pò di pazienza e io te lo dimostrerò, perché in difesa di Dio c'è altro da dire.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Prenderò da lontano il mio sapere e renderò giustizia al mio creatore,
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
poiché non è certo menzogna il mio parlare: un uomo di perfetta scienza è qui con te.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Ecco, Dio è grande e non si ritratta, egli è grande per fermezza di cuore.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Non lascia vivere l'iniquo e rende giustizia ai miseri.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Non toglie gli occhi dai giusti, li fa sedere sul trono con i re e li esalta per sempre.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Se talvolta essi sono avvinti in catene, se sono stretti dai lacci dell'afflizione,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
fa loro conoscere le opere loro e i loro falli, perché superbi;
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
apre loro gli orecchi per la correzione e ordina che si allontanino dalla iniquità.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
Se ascoltano e si sottomettono, chiuderanno i loro giorni nel benessere e i loro anni nelle delizie.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Ma se non vorranno ascoltare, di morte violenta periranno, spireranno senza neppure saperlo.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
I perversi di cuore accumulano l'ira; non invocano aiuto, quando Dio li avvince in catene:
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
si spegne in gioventù la loro anima, e la loro vita all'età dei dissoluti.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Ma egli libera il povero con l'afflizione, gli apre l'udito con la sventura.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Anche te intende sottrarre dal morso dell'angustia: avrai in cambio un luogo ampio, non ristretto e la tua tavola sarà colma di vivande grasse.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
Ma se colmi la misura con giudizi da empio, giudizio e condanna ti seguiranno.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
La collera non ti trasporti alla bestemmia, l'abbondanza dell'espiazione non ti faccia fuorviare.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Può forse farti uscire dall'angustia il tuo grido, con tutti i tentativi di forza?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Non sospirare quella notte, in cui i popoli vanno al loro luogo.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Bada di non volgerti all'iniquità, poiché per questo sei stato provato dalla miseria.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Ecco, Dio è sublime nella sua potenza; chi come lui è temibile?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Chi mai gli ha imposto il suo modo d'agire o chi mai ha potuto dirgli: «Hai agito male?».
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Ricordati che devi esaltare la sua opera, che altri uomini hanno cantato.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Ogni uomo la contempla, il mortale la mira da lontano.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Ecco, Dio è così grande, che non lo comprendiamo: il numero dei suoi anni è incalcolabile.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Egli attrae in alto le gocce dell'acqua e scioglie in pioggia i suoi vapori,
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
che le nubi riversano e grondano sull'uomo in grande quantità.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Chi inoltre può comprendere la distesa delle nubi, i fragori della sua dimora?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Ecco, espande sopra di esso il suo vapore e copre le profondità del mare.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
In tal modo sostenta i popoli e offre alimento in abbondanza.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Arma le mani di folgori e le scaglia contro il bersaglio.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Lo annunzia il suo fragore, riserva d'ira contro l'iniquità.