< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Elihu aussi continua, et dit,
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
« Supporte-moi un peu, et je te montrerai; car j'ai encore quelque chose à dire au nom de Dieu.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
J'obtiendrai mes connaissances de loin, et j'attribuerai la justice à mon créateur.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
Car en vérité mes paroles ne sont pas fausses. Celui qui est parfait dans la connaissance est avec vous.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
« Voici, Dieu est puissant, et il ne méprise personne. Il est puissant par la force de son intelligence.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Il ne préserve pas la vie des méchants, mais rend justice aux affligés.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Il ne détourne pas ses yeux des justes, mais avec des rois sur le trône, il les fixe pour toujours, et ils sont exaltés.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
S'ils sont liés par des entraves, et sont pris dans les cordons de l'affliction,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
puis il leur montre leur travail, et leurs transgressions, qu'ils se sont comportés avec orgueil.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
Il ouvre aussi leurs oreilles à l'instruction, et ordonne qu'ils reviennent de l'iniquité.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
S'ils l'écoutent et le servent, ils passeront leurs jours dans la prospérité, et leurs années de plaisirs.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
Mais s'ils n'écoutent pas, ils périront par l'épée; ils mourront sans savoir.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
« Mais ceux dont le cœur est impie accumulent la colère. Ils ne crient pas à l'aide quand il les lie.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Ils meurent dans leur jeunesse. Leur vie périt parmi les impurs.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Il délivre les affligés par leur affliction, et ouvre leur oreille dans l'oppression.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Oui, il t'aurait attiré hors de la détresse, dans un endroit vaste, où il n'y a aucune restriction. Ce qui est mis sur votre table serait plein de graisse.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
« Mais vous êtes pleins du jugement des méchants. Le jugement et la justice s'emparent de vous.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
Ne laissez pas les richesses vous inciter à la colère, ne vous laissez pas détourner par la taille d'un pot-de-vin.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Tes richesses te soutiendraient-elles dans la détresse? ou de toute la puissance de ta force?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Ne désirez pas la nuit, quand les gens sont coupés à leur place.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Prenez garde, ne regardez pas l'iniquité; car vous avez choisi cela plutôt que l'affliction.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Voici que Dieu est exalté dans sa puissance. Qui est un enseignant comme lui?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Qui lui a prescrit sa voie? Ou qui peut dire: « Tu as commis l'iniquité »?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
« Souviens-toi que tu magnifies son œuvre, sur laquelle les hommes ont chanté.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Tous les hommes l'ont regardé. L'homme le voit de loin.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Voici, Dieu est grand, et nous ne le connaissons pas. Le nombre de ses années est insondable.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
Car il fait monter les gouttes d'eau, qui distillent en pluie de sa vapeur,
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
que les cieux déversent et qui tombent sur l'homme en abondance.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
En effet, quelqu'un peut-il comprendre la propagation des nuages et les tonnerres de son pavillon?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Voici qu'il répand sa lumière autour de lui. Il couvre le fond de la mer.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
Car c'est par eux qu'il juge le peuple. Il donne de la nourriture en abondance.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
Il couvre ses mains de la foudre, et lui ordonne de frapper la marque.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
Son bruit parle de lui, et le bétail aussi, au sujet de la tempête qui s'annonce.

< Yobu 36 >