< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
And Elius further continued, and said,
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Wait for me yet a little while, that I may teach you: for there is yet speech in me.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Having fetched my knowledge from afar, and according to my works,
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
I will speak just things truly, and you shall not unjustly receive unjust words.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
But know that the Lord will not cast off an innocent man: being mighty in strength of wisdom,
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
he will not by any means save alive the ungodly: and he will grant the judgment of the poor.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
He will not turn away his eyes from the righteous, but [they shall be] with kings on the throne: and he will establish them in triumph, and they shall be exalted.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
But they that are bound in fetters shall be holden in cords of poverty.
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
And he shall recount to them their works, and their transgressions, for such will act with violence.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
But he will listen to the righteous: and he has said that they shall turn from unrighteousness.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
If they should hear and serve [him], they shall spend their days in prosperity, and their years in honor.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
But he preserves not the ungodly; because they are not willing to know the Lord, and because when reproved they were disobedient.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
And the hypocrites in heart will array wrath [against themselves]; they will not cry, because he has bound them.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
Therefore let their soul die in youth, and their life be wounded by messengers [of death].
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
Because they afflicted the weak and helpless: and he will vindicate the judgment of the meek.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
And he has also enticed you out of the mouth of the enemy:
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
[there is] a deep gulf [and] a rushing stream beneath it, and your table came down full of fatness. Judgment shall not fail from the righteous;
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
but there shall be wrath upon the ungodly, by reason of the ungodliness of the bribes which they received for iniquities.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Let not [your] mind willingly turn you aside from the petition of the feeble that are in distress.
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
And draw not forth all the mighty [men] by night, so that the people should go up instead of them.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
But take heed lest you do that which is wrong: for of this you has made choice because of poverty.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Behold, the Mighty One shall prevail by his strength: for who is powerful as he is?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
And who is he that examines his works? or who can say, he has wrought injustice?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Remember that his works are great [beyond] those which men have attempted.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
Every man has seen in himself, how many mortals are wounded.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Behold, the Mighty One is great, and we shall not know [him]: the number of his years is even infinite.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
And the drops of rain are numbered by him, and shall be poured out in rain to form a cloud.
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
The ancient [heavens] shall flow, and the clouds overshadow innumerable mortals: he has fixed a time to cattle, and they know the order of rest. [Yet] by all these things your understanding is not astonished, neither is your mind disturbed in [your] body.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
And though one should understand the outspreadings of the clouds, [or] the measure of his tabernacle;
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
behold he will stretch his bow against him, and he covers the bottom of the sea.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
For by them he will judge the nations: he will give food to him that has strength.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
He has hidden the light in [his] hands, and given charge concerning it to the interposing [cloud].
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
The Lord will declare concerning this [to] his friend: [but there is] a portion also for unrighteousness.

< Yobu 36 >