< Yobu 35 >
1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Y PROCEDIENDO Eliú en su razonamiento, dijo:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
¿Piensas ser conforme á derecho esto [que] dijiste: Más justo soy yo que Dios?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
Porque dijiste: ¿Qué ventaja sacarás tú de ello? ¿ó qué provecho tendré de mi pecado?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Yo te responderé razones, y á tus compañeros contigo.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Mira á los cielos, y ve, y considera que las nubes son más altas que tú.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Si pecares, ¿qué habrás hecho contra él? y si tus rebeliones se multiplicaren, ¿qué le harás tú?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Si fueres justo, ¿qué le darás á él? ¿ó qué recibirá de tu mano?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Al hombre como tú [dañará] tu impiedad, y al hijo del hombre [aprovechará] tu justicia.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
A causa de la multitud de las violencias clamarán, y se lamentarán por el poderío de los grandes.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
Y ninguno dice: ¿Dónde está Dios mi Hacedor, que da canciones en la noche,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
Que nos enseña más que á las bestias de la tierra, y nos hace sabios más que las aves del cielo?
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Allí clamarán, y él no oirá, por la soberbia de los malos.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Ciertamente Dios no oirá la vanidad, ni la mirará el Omnipotente.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Aunque más digas, No lo mirará; haz juicio delante de él, y en él espera.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Mas ahora, porque en su ira no visita, ni conoce con rigor,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
por eso Job abrió su boca vanamente, y multiplica palabras sin sabiduría.