< Yobu 35 >
1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Moreover Elihu respondeu,
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
“Você acha que isto é um direito seu, ou você diz: “Minha justiça é mais do que a de Deus”?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
que você pergunta: 'Que vantagem será para você? Que lucro eu terei, mais do que se tivesse pecado”?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Eu lhe responderei, e seus companheiros com você.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Olhe para os céus, e veja. Veja os céus, que são mais altos do que você.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Se você pecou, que efeito você tem contra ele? Se suas transgressões são multiplicadas, o que você faz com ele?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Se você é justo, o que você lhe dá? Ou o que ele recebe de sua mão?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Sua perversidade pode ferir um homem como você é, e sua retidão pode beneficiar um filho do homem.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
“Por causa da multidão de opressões que eles gritam. Eles clamam por ajuda por causa do braço do poderoso.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
Mas ninguém diz: 'Onde está Deus, meu Criador', que dá canções durante a noite,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
que nos ensina mais do que os animais da terra, e nos faz mais sábios que as aves do céu”...
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Lá eles choram, mas ninguém responde, por causa do orgulho dos homens maus.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Certamente Deus não vai ouvir um grito vazio, nem o Todo-Poderoso o considerará.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Quanto menos quando você diz que não o vê. A causa está diante dele, e você espera por ele!
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Mas agora, porque ele não o visitou em sua raiva, nem considera muito a arrogância,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
therefore Trabalho abre sua boca com a conversa vazia, e ele multiplica as palavras sem conhecimento”.