< Yobu 35 >
1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Elihu mówił dalej:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Czy uważasz to za słuszne, że powiedziałeś: Mam więcej sprawiedliwości niż Bóg?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
Powiedziałeś bowiem: Cóż mi pomoże? Jaki będę miał pożytek [z tego, że zostanę] oczyszczony z grzechu?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Odpowiem dowodnie tobie i twoim towarzyszom wraz z tobą.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Spójrz w niebo i zobacz, przypatrz się obłokom, które są wyżej od ciebie.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Jeśli zgrzeszysz, co zrobisz przeciwko niemu? A jeśli pomnożą się twoje nieprawości, co mu uczynisz?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Jeśli jesteś sprawiedliwy, co mu dajesz? Albo co otrzymuje z twojej ręki?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Twoja niegodziwość [zaszkodzi] człowiekowi takiemu jak ty, a twoja sprawiedliwość [pomoże] synowi człowieka.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
[Ludzie] krzyczą z powodu mnóstwa ucisków, wołają z powodu ramienia mocarzy.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
[Ale] nikt nie mówi: Gdzie jest Bóg, mój Stwórca, który w nocy daje pieśni;
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
Ten, który uczy nas więcej niż zwierzęta ziemskie i czyni nas mądrzejszymi od ptactwa niebieskiego?
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Tak więc wołają, ale nikt nie wysłuchuje z powodu pychy złych ludzi.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Doprawdy, Bóg nie wysłucha [słów] obłudy, Wszechmocny na nią nie zważa.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Chociaż mówisz, że go nie widzisz, sąd jest przed nim, więc mu zaufaj.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Teraz jednak jego gniew spadł na ciebie w niewielkim stopniu, jakby nie znał wielkości twoich [grzechów].
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
Dlatego Hiob na próżno otwiera swe usta; mnoży słowa bez poznania.