< Yobu 35 >

1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Igitur Eliu hæc rursum locutus est:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
[Numquid æqua tibi videtur tua cogitatio, ut diceres: Justior sum Deo?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
Dixisti enim: Non tibi placet quod rectum est: vel quid tibi proderit, si ego peccavero?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Itaque ego respondebo sermonibus tuis, et amicis tuis tecum.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Suspice cælum, et intuere: et contemplare æthera quod altior te sit.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Si peccaveris, quid ei nocebis? et si multiplicatæ fuerint iniquitates tuæ, quid facies contra eum?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Porro si juste egeris, quid donabis ei? aut quid de manu tua accipiet?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Homini qui similis tui est, nocebit impietas tua: et filium hominis adjuvabit justitia tua.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
Propter multitudinem calumniatorum clamabunt, et ejulabunt propter vim brachii tyrannorum.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
Et non dixit: Ubi est Deus qui fecit me, qui dedit carmina in nocte;
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
qui docet nos super jumenta terræ, et super volucres cæli erudit nos?
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Ibi clamabunt, et non exaudiet, propter superbiam malorum.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Non ergo frustra audiet Deus, et Omnipotens causas singulorum intuebitur.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Etiam cum dixeris: Non considerat: judicare coram illo, et expecta eum.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Nunc enim non infert furorem suum, nec ulciscitur scelus valde.
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
Ergo Job frustra aperit os suum, et absque scientia verba multiplicat.]

< Yobu 35 >