< Yobu 35 >

1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Und Elihu hob wieder an und sprach:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Hältst du das für recht? Du hast gesagt: Meine Gerechtigkeit ist größer als diejenige Gottes. [El]
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
Denn du fragst, was sie dir nütze; was gewinne ich mehr, als wenn ich gesündigt hätte? -
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Ich will dir Worte erwidern und deinen Genossen mit dir.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Blicke gen Himmel und sieh, und schaue die Wolken [Das hebr. Wort bezeichnet eigentl. die dünnen Luftschichten oberhalb der schweren Wolken, dann auch das Himmelsgewölbe; vergl. Kap. 37,18. 21] an, -sie sind höher als du.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Wenn du sündigst, was tust du ihm an? und mehren sich deine Übertretungen, was fügst du ihm zu?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Wenn du gerecht bist, was gibst du ihm, oder was empfängt er aus deiner Hand?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Für einen Mann wie du gilt deine Gesetzlosigkeit etwas, und für ein Menschenkind deine Gerechtigkeit.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
Wegen der Menge der Bedrückungen schreit man; man ruft um Hülfe wegen des Armes der Großen.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
Aber man spricht nicht: Wo ist Gott, mein Schöpfer, der Gesänge gibt in der Nacht,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
der uns mehr belehrt als die Tiere der Erde, und uns weiser macht als das [O. uns belehrt durch die Tiere, weise macht durch das usw.; vergl. Kap. 12,7] Gevögel des Himmels?
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Alsdann schreit man, wegen des Hochmuts der Bösen, aber er antwortet nicht.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Auf nur Eitles hört Gott [El] nicht, und der Allmächtige schaut es nicht an.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Wenn du auch sagst, du schauest ihn nicht-die Rechtssache ist vor ihm; so harre sein.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Und nun, wenn sein Zorn nicht heimgesucht hat, sollte er nicht sehr wohl um den Übermut wissen?
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
Und so sperrt Hiob eitler Weise seinen Mund auf, häuft Worte ohne Erkenntnis.

< Yobu 35 >