< Yobu 35 >

1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Moreover Elihu answered and said,
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Thinkest thou this to be right, that thou saidst, My righteousness is more than God's?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
For thou hast asked of what profit it is unto thee: what do I gain more than if I had sinned?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
I will reply to thee in words, and to thy companions with thee.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Look unto the heavens and see; and survey the skies: they are higher than thou.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
If thou sinnest, what doest thou against him? If thy transgressions be multiplied, what doest thou unto him?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
If thou be righteous, what givest thou to him? or what doth he receive of thy hand?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Thy wickedness [may affect] a man as thou [art], and thy righteousness a son of man.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
By reason of the multitude of oppressions they cry; they cry out by reason of the arm of the mighty:
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
But none saith, Where is God my Maker, who giveth songs in the night,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
Who teacheth us more than the beasts of the earth, and maketh us wiser than the fowl of the heavens?
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
There they cry, and he answereth not, because of the pride of evil men.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Surely God will not hear vanity, neither will the Almighty regard it.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Although thou sayest thou dost not see him, judgment is before him, therefore wait for him.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
But now, because he hath not visited in his anger, doth not [Job] know [his] great arrogancy?
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
For Job hath opened his mouth in vanity, and made words abundant without knowledge.

< Yobu 35 >