< Yobu 35 >
1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Moreover Elihu answered,
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
“Do you think this to be your right, or do you say, ‘My righteousness is more than God’s,’
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
that you ask, ‘What advantage will it be to you? What profit will I have, more than if I had sinned?’
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
I will answer you, and your companions with you.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Look to the skies, and see. See the skies, which are higher than you.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
If you have sinned, what effect do you have against him? If your transgressions are multiplied, what do you do to him?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
If you are righteous, what do you give him? Or what does he receive from your hand?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Your wickedness may hurt a man as you are, and your righteousness may profit a son of man.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
“By reason of the multitude of oppressions they cry out. They cry for help by reason of the arm of the mighty.
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
But no one says, ‘Where is God my Maker, who gives songs in the night,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
who teaches us more than the animals of the earth, and makes us wiser than the birds of the sky?’
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
There they cry, but no one answers, because of the pride of evil men.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
Surely God will not hear an empty cry, neither will the Almighty regard it.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
How much less when you say you do not see him. The cause is before him, and you wait for him!
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
But now, because he has not visited in his anger, neither does he greatly regard arrogance,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
therefore Job opens his mouth with empty talk, and he multiplies words without knowledge.”