< Yobu 35 >

1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Og Elihu tog til Orde og sagde:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
"Holder du det for Ret, og kalder du det din Ret for Gud,
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
at du siger: "Hvad båder det mig, hvad hjælper det mig, at jeg ikke synder?"
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Jeg vil give dig Svar og tillige med dig dine Venner:
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Løft dit Blik imod Himlen og se, læg Mærke til Skyerne, hvor højt de, er over dig!
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Hvis du synder, hvad skader du ham? Er din Brøde svar, hvad gør det da ham?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Er du retfærdig, hvad gavner du ham, hvad mon han får af din Hånd?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Du Menneske, dig vedkommer din Gudløshed, dig, et Menneskebarn, din Retfærd!
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
Man skriger over den megen Vold, råber om Hjælp mod de mægtiges Arm,
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
men siger ej: "Hvor er Gud, vor Skaber, som giver Lovsang om Natten,
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
lærer os mer end Jordens Dyr, gør os vise fremfor Himlens Fugle?"
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Der råber man, uden at han giver Svar, over de ondes Hovmod;
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
til visse, Gud hører ej tomme Ord, den Almægtige ænser dem ikke,
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
endsige din Påstand om ikke at se ham! Vær stille for hans Åsyn og bi på ham!
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Men nu, da hans Vrede ej bringer Straf og han ikke bekymrer sig stort om Synd,
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
så oplader Job sin Mund med Tant, uden Indsigt taler han store Ord.

< Yobu 35 >