< Yobu 35 >

1 Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
Ještě mluvil Elihu, a řekl:
2 “Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
Domníváš-liž se, že jsi to s soudem řekl: Spravedlnost má převyšuje Boží?
3 Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
Nebo jsi řekl: Co mi prospěje, jaký užitek budu míti, bych i nehřešil?
4 “Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
Já odpovím tobě místně, i tovaryšům tvým s tebou.
5 Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
Pohleď na nebe a viz, anobrž spatř oblaky, vyšší, než-lis ty.
6 Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
Jestliže bys hřešil, co svedeš proti němu? A byť se i rozmnožily nešlechetnosti tvé, co mu uškodíš?
7 Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
Budeš-li spravedlivý, čeho mu udělíš? Aneb co z ruky tvé vezme?
8 Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
Každémuť člověku bezbožnost jeho uškodí, a synu člověka spravedlnost jeho prospěje.
9 “Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
Z množství nátisk trpících, kteréž k tomu přivodí, aby úpěli a křičeli pro ukrutnost povýšených,
10 Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
Žádný neříká: Kde jest Bůh stvořitel můj? Ješto on dává zpěv i v noci.
11 amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
On vyučuje nás nad hovada zemská, a nad ptactvo nebeské moudřejší nás činí.
12 Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
Tehdáž volají-li pro pýchu zlých, nebývají vyslyšáni.
13 Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
A jistě žeť ošemetnosti nevyslýchá Bůh silný, a Všemohoucí nepatří na ni.
14 Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
Mnohem méně, jestliže díš: Nepatříš na to. Sám s sebou vejdi v soud před ním, a doufej v něho.
15 ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
Ale nyní poněvadž nic není těch věcí, navštívil jej hněv jeho; nebo nechce znáti hojnosti této veliké.
16 abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”
A protož marně Job otvírá ústa svá, hloupě rozmnožuje řeči své.

< Yobu 35 >