< Yobu 34 >
1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Y respondió Eliú, y dijo:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Oíd sabios, mis palabras, y doctos escuchádme:
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Porque el oído prueba las palabras, y el paladar gusta para comer.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Escojamos para vosotros el juicio, conozcamos entre nosotros cual sea lo bueno.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Porque Job ha dicho: Yo soy justo, y Dios me ha quitado mi derecho.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
En mi juicio yo fui mentiroso, mi saeta es gravada sin haber yo prevaricado.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
¿Qué hombre hay como Job, que bebe el escarnio como agua?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Y va en compañía con los que obran iniquidad, y anda con los hombres maliciosos.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Porque dijo: De nada servirá al hombre, si conformare su voluntad con Dios.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Por tanto varones de seso, oídme: Lejos vaya de Dios la impiedad, y del Omnipotente la iniquidad.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Porque él pagará al hombre su obra, y él le hará hallar conforme a su camino,
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Además de esto, cierto Dios no hará injusticia, y el Omnipotente no pervertirá el derecho.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
¿Quién visitó por él la tierra? ¿y quién puso en orden todo el mundo?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Si él pusiese sobre el hombre su corazón, y recogiese a sí su espíritu y su aliento,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Toda carne perecería juntamente, y el hombre se tornaría en polvo.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Y si hay en ti entendimiento, oye esto: escucha la voz de mis palabras.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
¿Enseñorearse ha el que aborrece juicio? ¿y condenarás al poderoso siendo justo?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
¿Decirse ha al rey: Perverso eres; y a los príncipes: Impíos sois?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
¿ Cuánto menos a aquel que no hace acepción de personas de príncipes, ni el rico es de él más respetado que el pobre? porque todos son obras de sus manos.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
En un momento mueren, y a media noche se alborotarán los pueblos, y pasarán, y sin mano será quitado el poderoso.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Porque sus ojos están sobre los caminos del hombre, y todos sus pasos ve.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
No hay tinieblas, ni sombra de muerte, donde se encubran los que obran maldad.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Porque nunca más permitirá al hombre, que vaya con Dios a juicio.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Él quebrantará a los fuertes sin pesquisa: y hará estar otros en lugar de ellos.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Por tanto él hará notorias las obras de ellos; y volverá la noche, y serán quebrantados.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Como a malos los herirá en lugar donde sean vistos.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Por cuanto se apartaron de él así, y no consideraron todos sus caminos:
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Haciendo venir delante de sí el clamor del pobre, y oyendo el clamor de los necesitados.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Y si él diere reposo, ¿quién inquietará? Si escondiere el rostro, ¿quién le mirará? Esto sobre una nación, y asimismo sobre un hombre:
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Haciendo que reine el hombre hipócrita para escándalos del pueblo.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Porque de Dios es decir: Yo perdoné, no destruiré.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Enséñame tú lo que yo no veo: que si hice mal, no lo haré más.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
¿ Ha de ser eso según tu mente? Él te recompensará, que no quieras tú, o quieras, y no yo: di lo que sabes.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Los hombres de seso dirán conmigo, y el hombre sabio me oirá.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Job no habla con sabiduría, y sus palabras no son con entendimiento.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Deseo que Job sea probado luengamente: para que haya respuestas contra los varones inicuos.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Por cuanto a su pecado añadió impiedad: bate las manos entre nosotros, y multiplica sus palabras contra Dios.