< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Eliú continuó:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Escuchen, oh sabios, mis palabras, y ustedes, los que saben, escúchenme.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Porque el oído distingue las palabras y el paladar prueba el alimento.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Escojamos lo que es recto y sepamos entre nosotros lo que es bueno.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Porque Job dijo: Yo soy justo. ʼEL me quitó mi derecho.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
¿Debo mentir con respecto a mi derecho? Aunque no cometí transgresión, mi herida es incurable.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
¿Quién hay como Job, quien bebe el desprecio como agua,
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
quien se va en compañía con los transgresores y camina con los perversos?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Pues afirma: De nada le sirve al hombre deleitarse en ʼElohim.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Por tanto, hombres cuerdos, escúchenme: ¡Lejos esté de ʼElohim la perversidad, y de ʼEL-Shadday la injusticia!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Porque Él paga al hombre según sus obras y hace que cada uno halle según su camino.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Ciertamente ʼElohim no obra perversamente, ni ʼEL-Shadday pervierte la justicia.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
¿Quién le dio autoridad sobre la tierra? ¿Quién le confió todo el universo?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Si Él determina hacer así, retirar para Sí mismo su Espíritu y su aliento,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
toda carne perecería juntamente, y el hombre volvería al polvo.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Si tienes entendimiento, escucha esto, escucha el sonido de mis palabras:
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
¿Gobernará el que aborrece la justicia? ¿Te atreves a condenar al Justo poderoso,
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
a Aquél que declara a un rey inútil y perversos a los nobles,
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Quien no muestra parcialidad con príncipes, ni considera al rico por encima del pobre? Porque todos ellos son la obra de sus manos.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
De repente a medianoche mueren, las gentes se estremecen y ya no están. Los poderosos son derribados y no por mano.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Porque los ojos de Él están sobre las sendas del hombre y observan todos sus pasos.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
No hay oscuridad ni sombras donde puedan ocultarse los que hacen iniquidad.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Pues no le impone plazo al hombre, para que comparezca a juicio ante ʼEL.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Él quebranta a los poderosos sin indagar y pone a otros en lugar de ellos.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Por cuanto conoce las obras de ellos, los trastorna en una noche, y quedan deshechos.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Los azota por sus perversidades en un lugar público,
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
porque se apartaron de seguirlo. No consideraron alguno de los caminos de Él.
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Buscaron que el clamor del pobre llegara a Él, y que escuchara el clamor de los afligidos.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Cuando Él da tranquilidad, ¿quién entonces lo inculpará? Si esconde su rostro, ¿quién lo mirará? Esto ocurre tanto con respecto a una nación como con respecto a un hombre,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
para evitar que reine el impío e imponga trampas al pueblo.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Porque, ¿alguno le dijo a ʼEL: Generé mi castigo, no pecaré más,
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
enséñame Tú lo que yo no veo? ¡Si obré mal, no lo haré más!
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
¿Retribuirá según tus condiciones, porque tú rechazas las de Él? Si rechazas o si aceptas, Él te retribuirá, no yo. Y si no es así, dí lo que sabes.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Los hombres de entendimiento me lo dirán, y el hombre sabio que me escucha:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Que Job no habló con sabiduría, que sus palabras fueron sin discernimiento,
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
que Job debe ser probado hasta el límite, porque respondió como los perversos,
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
y a su pecado añade rebelión. Bate palmas ante nosotros y multiplica sus palabras contra ʼEL.

< Yobu 34 >