< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Још говори Елијуј и рече:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Чујте, мудри, беседу моју, и разумни послушајте ме.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Јер ухо познаје беседу као што грло куша јело.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Разаберимо шта је право, извидимо међу собом шта је добро.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Јер Јов рече: Праведан сам, а Бог одбаци моју правду.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Хоћу ли лагати за своју правду? Стрела је моја смртна, а без кривице.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Који је човек као Јов да као воду пије подсмех?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
И да се дружи с онима који чине безакоње, и да ходи с безбожним људима?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Јер рече: Не помаже човеку да угађа Богу.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Зато, људи разумни, послушајте ме; далеко је од Бога злоћа и неправда од Свемогућег.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Јер по делу плаћа човеку и даје сваком да нађе према путу свом.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Доиста Бог не ради зло и Свемогући не изврће правде.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Ко Му је предао земљу? И ко је уредио васиљену?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Кад би на себе окренуо срце своје, узео би к себи дух свој и дисање своје;
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Изгинуло би свако тело, и човек би се вратио у прах.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Ако си, дакле, разуман, чуј ово: слушај глас речи мојих.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Може ли владати онај који мрзи на правду? Хоћеш ли осудити оног који је најправеднији?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Каже ли се цару: Ниткове! И кнезовима: Безбожници?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
А камо ли Ономе који не гледа кнезовима ко су, нити у Њега вреди више богати од сиромаха, јер су сви дело руку Његових.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Умиру за час, и у по ноћи усколеба се народ и пропадне, и однесе се јаки без руке људске.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Јер су очи Његове обраћене на путеве човечије и види све кораке његове.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Нема мрака ни сена смртнога где би се сакрили који чине безакоње.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Јер никоме не одгађа кад дође да се суди с Богом.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Сатире јаке недокучиво, и поставља друге на њихово место.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Јер зна дела њихова, и док обрати ноћ, сатру се.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Као безбожне разбија их на видику.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Јер одступише од Њега и не гледаше ни на које путеве Његове;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Те дође до Њега вика сиромахова, и чу вику невољних.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Кад Он умири, ко ће узнемирити? И кад Он сакрије лице, ко ће Га видети? И то бива и народу и човеку.
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Да не би царовао лицемер, да не би било замке народу.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Заиста, треба казати Богу: Подносио сам, нећу више грешити.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
А шта не видим, Ти ме научи; ако сам чинио неправду, нећу више.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Еда ли ће по теби плаћати, јер теби није по вољи, јер ти бираш а не Он? Ако знаш шта, говори.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Људи ће разумни са мном казати, и мудар ће човек пристати,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Да Јов не говори разумно, и да речи његове нису мудре.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Оче мој, нека се Јов искуша до краја, што одговара као зли људи.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Јер домеће на грех свој безакоње, пљеска рукама међу нама, и много говори на Бога.

< Yobu 34 >