< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Елиху а луат дин ноу кувынтул ши а зис:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
„Аскултаць, ынцелепцилор, кувинтеле меле! Луаць аминте ла мине, причепуцилор!
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Кэч урекя деосебеште кувинтеле кум густэ черул гурий букателе.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Сэ алеӂем че есте дрепт, сэ ведем ынтре ной че есте бун.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Йов а зис: ‘Сунт невиноват Ши Думнезеу ну вря сэ-мь дя дрептате;
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
ам дрептате ши трек дрепт минчинос; рана мя есте жалникэ, ши сунт фэрэ пэкат.’
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Есте вреун ом ка Йов, каре сэ бя батжокура ка апа,
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
каре сэ умбле ын товэрэшия челор че фак рэу, каре сэ мяргэ мынэ ын мынэ ку чей нелеӂюиць?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Кэч ел а зис: ‘Ну-й фолосеште нимик омулуй сэ-шь пунэ плэчеря ын Думнезеу.’
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Аскултаци-мэ дар, оамень причепуць! Департе де Думнезеу недрептатя, департе де Чел Атотпутерник фэрэделеӂя!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Ел дэ омулуй дупэ фаптеле луй, рэсплэтеште фиекэруя дупэ кэиле луй.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Ну, негрешит, Думнезеу ну сэвыршеште фэрэделеӂя; Чел Атотпутерник ну калкэ дрептатя.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Чине Л-а ынсэрчинат сэ кырмуяскэ пэмынтул? Чине Й-а дат лумя ын грижа Луй?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Дакэ ну с-ар гынди декыт ла Ел, дакэ Шь-ар луа ынапой духул ши суфларя,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
тот че есте карне ар пери деодатэ ши омул с-ар ынтоарче ын цэрынэ.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Дакэ ай причепере, аскултэ лукрул ачеста, я аминте ла гласул кувинтелор меле!
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Оаре ар путя сэ домняскэ ун врэжмаш ал дрептэций? Ши вей осынди ту пе Чел дрепт, пе Чел путерник,
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
каре стригэ кэтре ымпэраць: ‘Нетребничилор!’ Ши кэтре домниторь: ‘Нелеӂюицилор!’,
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
каре ну каутэ ла фаца челор марь ши ну фаче деосебире ынтре богат ши сэрак, пентру кэ тоць сунт лукраря мынилор Луй?
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Ынтр-о клипэ, ей ышь перд вяца. Ла мезул нопций, ун попор се клатинэ ши пере. Чел путерник пере, фэрэ аместекул мыний вреунуй ом.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Кэч Думнезеу веде пуртаря тутурор, привеште паший фиекэруя.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Ну есте нич ынтунерик, нич умбрэ а морций унде сэ се поатэ аскунде чей че фак фэрэделеӂя.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Думнезеу н-аре невое сэ привяскэ мултэ време ка сэ трагэ пе ун ом ла жудекатэ ынаинтя Луй.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Ел здробеште пе чей марь фэрэ черчетаре ши пуне пе алций ын локул лор.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Кэч Ел куноаште фаптеле лор: ноаптя ый рэстоарнэ, сунт здробиць.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Ый ловеште ка пе ниште нелеӂюиць ын фаца тутурор.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Абэтынду-се де ла Ел ши пэрэсинд тоате кэиле Луй,
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
ей ау фэкут сэ се ыналце ла Думнезеу стригэтул сэракулуй. Й-ау ындрептат луаря аминте ла стригэтул челуй ненорочит.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Дакэ дэ Ел паче, чине поате с-о тулбуре? Дакэ Ышь аскунде Ел Фаца, чине поате сэ-Л вадэ? Ла фел Се поартэ фие ку ун попор, фие ку ун ом,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
пентру ка нелеӂюитул сэ ну май стэпыняскэ ши сэ ну май фие о курсэ пентру попор.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Кэч а зис ел вреодатэ луй Думнезеу: ‘Ам фост педепсит, ну вой май пэкэтуи;
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
аратэ-мь че ну вэд; дакэ ам фэкут недрептэць, ну вой май фаче’?
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Оаре дупэ пэреря та ва фаче Думнезеу дрептате? Ту лепезь, ту алеӂь, ши ну еу; Спуне дар че штий!
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Оамений ку причепере вор фи де пэреря мя, ынцелептул каре м-аскултэ ва гынди ка мине:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Йов ворбеште фэрэ причепере, ши кувынтэриле луй сунт липсите де жудекатэ.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Сэ фие ынчеркат дар май департе, фииндкэ рэспунде ка чей рэй!
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Кэч адаугэ ла грешелиле луй пэкате ной; бате дин палме ын мижлокул ностру, ышь ынмулцеште кувинтеле ымпотрива луй Думнезеу.”

< Yobu 34 >