< Yobu 34 >
1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Elihu mówił dalej:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Słuchajcie, mądrzy, moich słów i wy, uczeni, posłuchajcie mnie.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Ucho bowiem bada słowa, jak podniebienie smakuje pokarm.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Wybierzmy sobie sąd, rozeznajmy między sobą, co jest dobre.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Hiob bowiem powiedział: Jestem sprawiedliwy, a Bóg odrzucił moją sprawę.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Czy mam kłamać wbrew swojej racji? Nieuleczalna jest moja rana, bez przestępstwa.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Czy jest człowiek podobny do Hioba, który pije obelgi jak wodę?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
I który obraca się w towarzystwie czyniących nieprawość i chodzi z niegodziwcami?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Powiedział bowiem: Nic to nie pomoże człowiekowi, że ma upodobanie w Bogu.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Dlatego posłuchajcie mnie, ludzie rozumni: Daleki jest Bóg od niegodziwości, Wszechmocny – od nieprawości.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Bo odpłaci człowiekowi według jego czynu i wynagrodzi każdemu według jego drogi.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Nie, naprawdę Bóg nie czyni przewrotnie, Wszechmocny nie wypacza sądu.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Któż mu powierzył ziemię? Kto urządził cały okrąg świata?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Gdyby zwrócił ku człowiekowi swoje serce, gdyby wziął do siebie jego ducha i tchnienie;
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
To zginęłoby wszelkie ciało razem, a człowiek w proch by się obrócił.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Jeśli więc masz rozum, posłuchaj tego [i] nadstaw uszu na moje słowa.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Czy ma panować ten, który nienawidzi prawości? Czy potępisz tego, który jest bardzo sprawiedliwy?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Czy wypada do króla mówić: Nikczemniku? A do książąt: Bezbożni?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Tym bardziej do tego, który nie ma względu na książąt i nie stawia bogacza nad ubogim? Oni wszyscy bowiem są dziełem jego rąk.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Umrą nagle, o północy lud będzie wzruszony i przeminie, a mocarz zostanie usunięty bez [udziału] ręki [ludzkiej].
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Jego oczy bowiem patrzą na drogi człowieka i [on] widzi wszystkie jego kroki.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Nie ma ciemności ani cienia śmierci, gdzie mogliby się ukryć ci, którzy czynią nieprawość.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Na człowieka bowiem nie wkłada więcej [niż to, co słuszne], aby stawił się na sąd przed Bogiem.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Rozbije wielu mocarzy i innych osadzi w ich miejsce.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
A ponieważ zna ich czyny, wywraca ich w nocy, aby byli zmiażdżeni.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Chłoszcze ich jako niegodziwych w miejscu widocznym;
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Za to, że odstąpili od niego i nie zważali na żadne jego drogi;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Z tego powodu dochodzi do niego wołanie biednych, a on wysłuchuje wołania ubogich.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Gdy zaprowadzi pokój, któż go zburzy? A gdy zakryje swoje oblicze, któż go ujrzy? [A czyni] tak zarówno narodowi, jak i człowiekowi;
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Aby obłudnik już nie panował i nie był pułapką dla ludzi.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Doprawdy, powinieneś mówić do Boga: Poniosłem [karę], a nie będę [już] grzeszyć.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Naucz mnie tego, [czego] nie widzę; jeśli popełniłem nieprawość, [już] więcej tego nie uczynię.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Czy [wszystko] ma być po twojej myśli? On odpłaci, czy odrzucisz, czy wybierzesz, a nie ja. Ale jeśli wiesz lepiej, to powiedz.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Niech mi powiedzą ludzie rozumni, niech człowiek mądry posłucha mnie:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Hiob mówi niemądrze, a jego słowa nie są roztropne.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Niech Hiob zostanie doświadczony do końca za swoje odpowiedzi odnośnie do niegodziwych ludzi.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Dodaje bowiem buntu do swego grzechu, klaszcze przy nas rękoma i mnoży swoje słowa przeciwko Bogu.