< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Pronuncians itaque Eliu, etiam haec locutus est:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Audite sapientes verba mea, et eruditi auscultate me:
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Auris enim verba probat, et guttur escas gustu diiudicat.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Iudicium eligamus nobis, et inter nos videamus quid sit melius.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Quia dixit Iob: Iustus sum, et Deus subvertit iudicium meum.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
In iudicando enim me, mendacium est: violenta sagitta mea absque ullo peccato.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Quis est vir ut est Iob, qui bibit subsannationem quasi aquam:
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Qui graditur cum operantibus iniquitatem, et ambulat cum viris impiis?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Dixit enim: Non placebit vir Deo, etiam si cucurrerit cum eo.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Ideo viri cordati audite me, absit a Deo impietas, et ab Omnipotente iniquitas.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Opus enim hominis reddet ei, et iuxta vias singulorum restituet eis.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Vere enim Deus non condemnabit frustra, nec Omnipotens subvertet iudicium.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Quem constituit alium super terram? aut quem posuit super orbem, quem fabricatus est?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Si direxerit ad eum cor suum, spiritum illius et flatum ad se trahet.
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Deficiet omnis caro simul, et homo in cinerem revertetur.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Si habes ergo intellectum, audi quod dicitur, et ausculta vocem eloquii mei.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Numquid qui non amat iudicium, sanari potest? et quomodo tu eum, qui iustus est, in tantum condemnas?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Qui dicit regi, apostata: qui vocat duces impios:
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Qui non accipit personas principum: nec cognovit tyrannum, cum disceptaret contra pauperem: opus enim manuum eius sunt universi.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Subito morientur, et in media nocte turbabuntur populi, et pertransibunt, et auferent violentum absque manu.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Oculi enim eius super vias hominum, et omnes gressus eorum considerat.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Non sunt tenebrae, et non est umbra mortis, ut abscondantur ibi qui operantur iniquitatem.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Neque enim ultra in hominis potestate est, ut veniat ad Deum in iudicium.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Conteret multos, et innumerabiles, et stare faciet alios pro eis.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Novit enim opera eorum: et idcirco inducet noctem, et conterentur.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Quasi impios percussit eos in loco videntium.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Qui quasi de industria recesserunt ab eo, et omnes vias eius intelligere noluerunt:
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Ut pervenire facerent ad eum clamorem egeni, et audiret vocem pauperum.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Ipso enim concedente pacem, quis est qui condemnet? ex quo absconderit vultum, quis est qui contempletur eum et super gentes et super omnes homines?
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Qui regnare facit hominem hypocritam propter peccata populi.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Quia ergo ego locutus sum ad Deum, te quoque non prohibebo.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Si erravi, tu doce me: si iniquitatem locutus sum, ultra non addam.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Numquid a te Deus expetit eam, quia displicuit tibi? tu enim coepisti loqui, et non ego: quod si quid nosti melius, loquere.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Viri intelligentes loquantur mihi, et vir sapiens audiat me.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Iob autem stulte locutus est, et verba illius non sonant disciplinam.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Pater mi, probetur Iob usque ad finem: ne desinas ab homine iniquitatis.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Qui addit super peccata sua blasphemiam, inter nos interim constringatur: et tunc ad iudicium provocet sermonibus suis Deum.

< Yobu 34 >