< Yobu 34 >
1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
C’est pourquoi continuant son discours, Eliu dit encore ceci:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Sages, écoutez mes paroles, et vous, savants, prêtez-moi attention;
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Car l’oreille discerne les paroles comme le palais juge des mets par le goût.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Formons-nous un jugement, et voyons entre nous ce qu’il y a de mieux.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Job a dit: Je suis juste, et Dieu détruit mon bon droit.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Car dans le jugement porté contre moi, il y a fausseté: une flèche ardente m’a percé sans qu’il y ait en moi aucun péché.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Quel est l’homme comme est Job, qui boit la dérision comme l’eau;
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Qui marche avec ceux qui opèrent l’iniquité, et chemine avec les hommes impies?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Car il a dit: L’homme ne plaira pas à Dieu, quand même il aurait couru avec lui.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
C’est pourquoi, hommes sensés, écoutez-moi: Loin de Dieu l’impiété, et loin du Tout-Puissant l’iniquité!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Car il rendra à l’homme selon ses œuvres, et il traitera chacun selon ses voies.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Certainement Dieu ne condamnera pas sans sujet, et le Tout-Puissant ne détruira pas le bon droit.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Quel autre que lui a-t-il constitué sur la terre? ou qui a-t-il établi sur l’univers, qu’il a formé?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
S’il dirigeait vers lui son cœur, il attirerait à soi son esprit et son souffle.
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Toute chair périrait en même temps, et l’homme retournerait en cendre.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Si donc tu as l’intelligence, écoute ce que l’on dit, et sois attentif à mes paroles.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Est-ce que celui qui n’aime pas la justice, peut être guéri? et comment toi condamnes-tu si hautement celui qui est juste?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Celui qui dit à un roi: Apostat; qui appelle les grands impies;
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Qui ne fait point acception de la personne des princes, qui n’a pas connu un tyran, lorsqu’il disputait contre un pauvre, parce que tous les hommes sont l’ouvrage de ses mains.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Ils mourront tout à coup, et au milieu de la nuit les peuples se troubleront, ils passeront et le violent sera emporté sans la main de l’homme.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Car les yeux de Dieu sont sur les voies des hommes, et il considère tous leurs pas.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Il n’y a pas de ténèbres, et il n’y a pas d’ombre de mort, où puissent se cacher ceux qui opèrent l’iniquité.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Car il n’est plus au pouvoir de l’homme de venir devant Dieu en jugement.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Il en brisera une multitude innombrable, et il en établira d’autres à leur place.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Car il connaît leurs œuvres, et c’est pourquoi il fera venir la nuit, et ils seront brisés.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Il les a frappés comme impies, dans un lieu où on les voyait.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Eux qui, de propos délibéré, se sont retirés de lui, et n’ont pas voulu comprendre toutes ses voies;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
En sorte qu’ils ont fait parvenir jusqu’à lui le cri de l’indigent, et qu’il a entendu la voix des pauvres.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Car, lui accordant la paix, qui est celui qui condamnera? et s’il cache son visage aux nations et à tous les hommes, qui est-ce qui pourra le contempler?
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
C’est lui qui fait régner un homme hypocrite, à cause des péchés du peuple.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Puis donc que j’ai parlé à Dieu, je ne t’empêcherai pas de parler aussi.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Si j’ai erré, instruis-moi; si j’ai parlé iniquité, je n’ajouterai plus rien.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
N’est-ce pas à toi que Dieu demande compte de cette iniquité qui t’a déplu? car c’est toi qui as commencé à parler, et non pas moi; si tu sais quelque chose de meilleur, parle.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Que des hommes intelligents me parlent, et qu’un homme sage m’écoute.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Pour Job, il a parlé follement, et ses paroles n’annoncent pas la science.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Mon père, que Job soit éprouvé jusqu’à la fin; ne cessez point de frapper un homme d’iniquité.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Parce qu’il ajoute à ses péchés le blasphème, qu’il soit, malgré cela, pressé par nos raisons; et qu’alors il appelle Dieu en jugement par ses discours.