< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Et Élihu reprit la parole et dit:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Sages, écoutez mes paroles, et vous qui avez de la connaissance, prêtez-moi l’oreille;
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Car l’oreille éprouve les discours, comme le palais goûte les aliments.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Choisissons pour nous ce qui est juste, et reconnaissons entre nous ce qui est bon.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Car Job a dit: Je suis juste, et Dieu a écarté mon droit;
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Mentirai-je contre ma droiture? ma blessure est incurable, sans qu’il y ait de transgression.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Qui est l’homme qui soit comme Job? Il boit la moquerie comme l’eau;
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Il marche dans la compagnie des ouvriers d’iniquité, et il chemine avec les hommes méchants.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Car il a dit: Il ne profite de rien à l’homme de trouver son plaisir en Dieu.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
C’est pourquoi, hommes de sens, écoutez-moi: Loin de Dieu la méchanceté, et loin du Tout-puissant l’iniquité!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Car il rendra à l’homme ce qu’il aura fait, et il fera trouver à chacun selon sa voie.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Certainement Dieu n’agit pas injustement, et le Tout-puissant ne pervertit pas le droit.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Qui a confié la terre à ses soins, et qui a placé le monde entier [sous lui]?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
S’il ne pensait qu’à lui-même et retirait à lui son esprit et son souffle,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Toute chair expirerait ensemble et l’homme retournerait à la poussière.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Si [tu as] de l’intelligence, écoute ceci; prête l’oreille à la voix de mes paroles.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Celui qui hait la justice gouvernera-t-il donc? Et condamneras-tu le juste par excellence?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Dira-t-on Bélial, au roi? – Méchants, aux nobles?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
[Combien moins] à celui qui ne fait pas acception de la personne des princes, et qui n’a pas égard au riche plutôt qu’au pauvre; car ils sont tous l’œuvre de ses mains.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Ils mourront en un moment; au milieu de la nuit les peuples chancellent et s’en vont, et les puissants sont retirés sans main.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Car ses yeux sont sur les voies de l’homme, et il voit tous ses pas.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Il n’y a pas de ténèbres, il n’y a pas d’ombre de la mort, où puissent se cacher les ouvriers d’iniquité.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Car il ne pense pas longtemps à un homme pour le faire venir devant Dieu en jugement.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Il brise les puissants, sans examen, et il fait que d’autres se tiennent à leur place;
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
En effet il connaît leurs œuvres: il les renverse de nuit, et ils sont écrasés.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Il les frappe comme des méchants dans le lieu où ils sont en vue,
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Parce qu’ils se sont retirés de lui, et qu’ils n’ont pas considéré toutes ses voies,
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Pour faire monter vers lui le cri du pauvre, en sorte qu’il entende le cri des malheureux.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Quand il donne la tranquillité, qui troublera? Il cache sa face, et qui le verra? [Il fait] ainsi, soit à une nation, soit à un homme,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Pour empêcher l’homme impie de régner, pour écarter du peuple les pièges.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Car a-t-il [jamais] dit à Dieu: Je porte ma peine, je ne ferai plus de mal;
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Ce que je ne vois pas, montre-le-moi; si j’ai commis l’iniquité, je ne le referai pas?
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Rétribuera-t-il selon tes pensées? car tu as rejeté [son jugement], car toi, tu as choisi, et non pas moi; ce que tu sais, dis-le donc.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Les hommes de sens me diront, et un homme sage qui m’écoute:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Job n’a pas parlé avec connaissance, et ses paroles ne sont pas intelligentes;
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Je voudrais que Job soit éprouvé jusqu’au bout, parce qu’il a répondu à la manière des hommes iniques;
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Car il a ajouté à son péché la transgression; il bat des mains parmi nous, et multiplie ses paroles contre Dieu.

< Yobu 34 >