< Yobu 34 >
1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
And Helyu pronounside, and spak also these thingis,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Wise men, here ye my wordis, and lerned men, herkne ye me; for the eere preueth wordis,
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
and the throte demeth metis bi taast.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Chese we doom to vs; and se we among vs, what is the betere.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
For Job seide, Y am iust, and God hath distried my doom.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
For whi lesynge is in demynge me, and myn arowe is violent with out ony synne.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Who is a man, as Joob is, that drynkith scornyng as watir?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
that goith with men worchynge wickidnesse, and goith with vnfeithful men?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
For he seide, A man schal not plese God, yhe, thouy he renneth with God.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Therfor ye men hertid, `that is, vndurstonde, here ye me; vnpite, `ethir cruelte, be fer fro God, and wickidnesse fro Almyyti God.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
For he schal yelde the werk of man to hym; and bi the weies of ech man he schal restore to hym.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
For verili God schal not condempne with out cause; nether Almyyti God schal distrie doom.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
What othere man hath he ordeyned on the lond? ether whom hath he set on the world, which he made?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
If God dressith his herte to hym, he schal drawe to hym silf his spirit and blast.
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Ech fleisch schal faile togidere; `and a man schal turne ayen in to aisch.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Therfor if thou hast vndurstondyng, here thou that that is seid, and herkne the vois of my speche.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Whether he that loueth not doom may be maad hool? and hou condempnest thou so myche him, that is iust?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Which seith to the kyng, Thou art apostata; which clepith the duykis vnpitouse, `ethir vnfeithful.
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
`Which takith not the persoones of princes, nether knew a tyraunt, whanne he stryuede ayens a pore man; for alle men ben the werk of hise hondis.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Thei schulen die sudeynli, and at mydnyyt puplis schulen be troblid, `ethir schulen be bowid, as othere bookis han; and schulen passe, and schulen take `awei `a violent man with out hond.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
For the iyen of God ben on the weies of men, and biholdith alle goyngis of hem.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
No derknessis ben, and no schadewe of deeth is, that thei, that worchen wickidnesse, be hid there;
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
for it is `no more in the power of man, that he come to God in to doom.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
God schal al to-breke many men and vnnoumbrable; and schal make othere men to stonde for hem.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
For he knowith the werkis of hem; therfor he schal brynge yn niyt, and thei schulen be al to-brokun.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
He smoot hem, as vnpitouse men, in the place of seinge men.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Whiche yeden awei fro hym bi `castyng afore, and nolden vndurstonde alle hise weies.
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
That thei schulden make the cry of a nedi man to come to hym, and that he schulde here the vois of pore men.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
For whanne he grauntith pees, who is that condempneth? Sithen he hidith his cheer, who is that seeth hym? And on folkis and on alle men `he hath power `to do siche thingis.
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Which makith `a man ypocrite to regne, for the synnes of the puple.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Therfor for Y haue spoke to God, also Y schal not forbede thee.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
If Y erride, teche thou me; if Y spak wickidnesse, Y schal no more adde.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Whether God axith that wickidnesse of thee, for it displeside thee? For thou hast bigunne to speke, and not Y; that if thou knowist ony thing betere, speke thou.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Men vndurstondynge, speke to me; and a wise man, here me.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Forsothe Joob spak folili, and hise wordis sownen not techyng.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
My fadir, be Joob preuede `til to the ende; ceesse thou not fro the man of wickidnesse,
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
`that addith blasfemye ouer hise synnes. Be he constreyned among vs in the meene tyme; and thanne bi hise wordis stire he God to the doom.