< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Furthermore Elihu answered and said,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Hear my words, O ye wise men; and give ear to me, ye that have knowledge.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
For the ear trieth words, as the mouth tasteth food.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Let us choose for ourselves what is right: let us know among ourselves what is good.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
For Job hath said, I am righteous: and God hath taken away my judgment.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Should I lie against my right? my wound is incurable without transgression.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
What man is like Job, who drinketh up scorning like water?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Who goeth in company with the workers of iniquity, and walketh with wicked men.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
For he hath said, It profiteth a man nothing that he should delight himself with God.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Therefore hearken to me, ye men of understanding: far be it from God, that he should do wickedness; and from the Almighty, that he should commit iniquity.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
For the work of a man he shall render to him, and cause every man to find according to his ways.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Yea, surely God will not do wickedly, neither will the Almighty pervert judgment.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Who hath given him a charge over the earth? or who hath disposed the whole world?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
If he should set his heart upon man, if he should gather to himself his spirit and his breath;
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
All flesh would perish together, and man would turn again to dust.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
If now thou hast understanding, hear this: hearken to the voice of my words.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Shall even he that hateth right govern? and wilt thou condemn him that is most just?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Is it fit to say to a king, Thou art wicked? and to princes, Ye are ungodly?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
How much less to him that accepteth not the persons of princes, nor regardeth the rich more than the poor? for they all are the work of his hands.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
In a moment they shall die, and the people shall be troubled at midnight, and pass away: and the mighty shall be taken away without hand.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
For his eyes are upon the ways of man, and he seeth all his goings.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
There is no darkness, nor shadow of death, where the workers of iniquity may hide themselves.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
For he will not lay upon man more than right; that he should enter into judgment with God.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
He shall break in pieces mighty men without number, and set others in their stead.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Therefore he knoweth their works, and he overturneth them in the night, so that they are destroyed.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
He striketh them as wicked men in the open sight of others;
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Because they turned back from him, and would not consider any of his ways:
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
So that they cause the cry of the poor to come to him, and he heareth the cry of the afflicted.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
When he giveth quietness, who then can make trouble? and when he hideth his face, who then can behold him? whether it be done against a nation, or against a man only:
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
That the hypocrite may not reign, lest the people should be ensnared.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Surely hast any one said to God, I have borne chastisement, I will not offend any more:
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
That which I see not teach thou me: if I have done iniquity, I will do no more.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Should it be according to thy mind? he will recompense it, whether thou shalt refuse, or whether thou shalt choose; and not I: therefore speak what thou knowest.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Let men of understanding tell me, and let a wise man hearken to me.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Job hath spoken without knowledge, and his words were without wisdom.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
My desire is that Job may be tried to the end because of his answers for wicked men.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
For he addeth rebellion to his sin, he clappeth his hands among us, and multiplieth his words against God.

< Yobu 34 >