< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
And Elihu proceeded, and said:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Hear my words, ye wise men! Give ear to me, ye that have knowledge!
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
For the ear trieth words, As the mouth tasteth meat.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Let us examine for ourselves what is right; Let us know among ourselves what is true.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Job hath said, “I am righteous, And God refuseth me justice.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Though I am innocent, I am made a liar; My wound is incurable, though I am free from transgression.”
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Where is the man like Job, Who drinketh impiety like water;
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Who goeth in company with evil-doers, And walketh with wicked men?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
For he hath said, “A man hath no advantage, When he delighteth himself in God.”
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Wherefore hearken to me, ye men of understanding! Far be iniquity from God; Yea, far be injustice from the Almighty!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
For what a man hath done he will requite him, And render to every one according to his deeds.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Surely God will not do iniquity, Nor will the Almighty pervert justice.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Who hath given him the charge of the earth? Or who hath created the whole world?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Should he set his heart against man, Should he take back his spirit and his breath,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Then would all flesh expire together; Yea, man would return to the dust.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
If thou hast understanding, hear this! Give ear to the voice of my words!
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Shall he, that hateth justice, govern? Wilt thou then condemn the just and mighty One?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Is it fit to say to a king, Thou art wicked; Or to princes, Ye are unrighteous?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
How much less to him that is not partial to princes, Nor regardeth the rich more than the poor? For they are all the work of his hands.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
In a moment they die; yea, at midnight Do the people stagger and pass away, And the mighty are destroyed without hand.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
For his eyes are upon the ways of man; He seeth all his steps.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
There is no darkness, nor shadow of death, Where evil-doers may hide themselves.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
He needeth not attend long to a man, That he may go into judgment before God;
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
He dasheth in pieces the mighty without inquiry, And setteth up others in their stead.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Therefore he knoweth their works, And in a night he overthroweth them, so that they are destroyed.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
On account of their wickedness he smiteth them, In the presence of many beholders;
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Because they turned away from him, And had no regard to his ways,
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
And caused the cry of the poor to come before him; For he heareth the cry of the oppressed.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
When he giveth rest, who can cause trouble? And when he hideth his face, Who can behold him?
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
So is it with nations and individuals alike! That the wicked may no more rule, And may not be snares to the people.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Surely thou shouldst say unto God, “I have received chastisement; I will no more offend;
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
What I see not, teach thou me! If I have done iniquity, I will do it no more.”
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Shall he recompense according to thy mind, Because thou refusest, or because thou choosest, and not he? Speak, if thou hast knowledge!
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Men of understanding, Wise men, who hear me, will say,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
“Job hath spoken without knowledge, And his words are without wisdom.”
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
I desire that Job may be tried to the last, For answering like wicked men.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
For he addeth impiety to his sin; He clappeth his hands among us, And multiplieth words against God.

< Yobu 34 >