< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Moreover Elihu answered and said,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Hear my words, ye wise [men]; and give ear unto me, ye that have knowledge.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
For the ear trieth words, as the palate tasteth food.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Let us choose for ourselves what is right; let us know among ourselves what is good!
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
For Job hath said, I am righteous, and God hath taken away my judgment:
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Should I lie against my right? My wound is incurable without transgression.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
What man is like Job? he drinketh up scorning like water,
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
And goeth in company with workers of iniquity, and walketh with wicked men.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
For he hath said, It profiteth not a man if he delight himself in God.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Therefore hearken unto me, ye men of understanding: Far be wickedness from God, and wrong from the Almighty!
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
For a man's work will he render to him, and cause every one to find according to [his] way.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Yea, surely, God acteth not wickedly, and the Almighty perverteth not judgment.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Who hath entrusted to him the earth? and who hath disposed the whole world?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
If he only thought of himself, [and] gathered unto him his spirit and his breath,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
All flesh would expire together, and man would return to the dust.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
If now [thou hast] understanding, hear this: give ear to the voice of my words!
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Should he that hateth right indeed govern? and wilt thou condemn the All-just?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Shall one say to a king, Belial? to nobles, Wicked?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
[How then to him] that accepteth not the persons of princes, nor regardeth the rich man more than the poor? for they are all the work of his hands.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
In a moment they die, even at midnight the people are convulsed and pass away; and the strong are taken away without hand.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
For his eyes are upon the ways of man, and he seeth all his steps.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
There is no darkness, nor shadow of death, where the workers of iniquity may hide themselves.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
For he doth not long consider a man, to bring him before God in judgment.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
He breaketh in pieces mighty men without inquiry, and setteth others in their stead;
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Since he knoweth their actions; and he overthroweth [them] in the night, and they are crushed.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
He striketh them as wicked men in the open sight of others,
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Because they have turned back from him, and would consider none of his ways;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
So that they cause the cry of the poor to come unto him, and he heareth the cry of the afflicted.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
When he giveth quietness, who then will disturb? and when he hideth [his] face, who shall behold him? and this towards a nation, or towards a man alike;
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
That the ungodly man reign not, that the people be not ensnared.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
For hath he said unto God, I bear [chastisement], I will not offend;
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
What I see not, teach thou me; if I have done wrong, I will do so no more?
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Shall he recompense according to thy mind? for thou hast refused [his judgment]; for thou so choosest, and not I; speak then what thou knowest.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Men of understanding will say to me, and a wise man who heareth me:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Job hath spoken without knowledge, and his words were not with intelligence.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Would that Job may be tried unto the end, because of [his] answers after the manner of evil men!
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
For he addeth rebellion unto his sin, he clappeth [his hands] among us, and multiplieth his words against God.

< Yobu 34 >