< Yobu 34 >
1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Elihoe vervolgde en sprak:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Gij wijzen, hoort naar mijn rede; Verstandigen, luistert naar mij:
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Want het oor toetst de woorden, Zoals het gehemelte spijzen keurt.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
We moeten zelf onderzoeken, wat recht is, Onder elkander beslissen wat goed is.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Want Job heeft gezegd: Ik ben rechtschapen, Maar God onthoudt mij mijn recht;
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Ondanks mijn recht moet ik lijden, Mijn wonde is ongeneeslijk, al ben ik niet schuldig!
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Is er wel iemand als Job, Die godslastering als water drinkt,
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
Die het gezelschap van boosdoeners opzoekt En met slechte lieden omgang heeft?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Want hij zegt: Wat baat het den mens, In God zijn behagen te stellen!
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Verstandige lieden, hoort dus naar mij: Onmogelijk; God doet geen kwaad, de Almachtige geen onrecht;
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Want Hij vergeldt de mensen hun daden, Behandelt iedereen naar zijn gedrag!
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Waarachtig, God kan geen onrecht begaan, De Almachtige het recht niet verkrachten!
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Wie heeft de aarde onder zijn leiding gesteld Wie Hem met de hele wereld belast?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Trekt Hij hun geest tot Zich terug, Neemt Hij tot Zich hun levensadem,
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Dan sterft onmiddellijk alle vlees, Keert de mens terug tot stof!
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Zijt ge verstandig, luister hiernaar, En leen het oor aan mijn rede:
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Kan Hij, die het recht zou haten, besturen; Kan de Alrechtvaardige onrecht bedrijven?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Hij, die tot den koning zegt: Belial Tot de edelen: Booswicht;
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Die vorsten niet voortrekt, Den arme niet achterstelt bij den rijke. Neen, ze zijn allen het werk zijner handen,
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
En sterven plotseling, midden in de nacht; Rijken worden opgeschrikt, en gaan heen, Machtigen verdwijnen, al steekt men er de hand niet naar uit.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Want zijn ogen zijn op de wegen der mensen gericht, En Hij ziet al hun schreden;
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Er bestaat geen duister of donker, Waarin de boosdoeners zich kunnen verbergen.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Neen, geen vaste tijd voor den mens, Om voor God ten gericht te verschijnen;
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Hij verplettert den machtige zonder verhoor, En stelt anderen voor hem in de plaats.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Hij geeft dus acht op hun daden, Hij stort ze omver in de nacht;
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Ze worden verbrijzeld tot straf voor hun boosheid, Hij tuchtigt ze op de plaats, waar allen het zien.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Want van Hem zijn ze afgeweken, En hebben op geen van zijn paden gelet;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Ze hebben het kermen der armen tot Hem doen komen, Zodat Hij het klagen der ellendigen hoort.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Hield Hij Zich stil, wie zou ze beschuldigen Bedekte Hij zijn gelaat, wie wees hen terecht? Neen, Hij houdt volk en eenling in het oog,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Opdat geen boze regeert, het volk niet zondigt.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Maar als de boze tot God zegt: Ik heb gedwaald, Doch ik wil niet meer zondigen;
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
Onderricht mij, totdat ik tot inzicht kom; Heb ik misdaan, ik doe het niet meer!
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Moet Hij, volgens u, het dan toch maar vergelden, Omdat gij zijn gerechtigheid anders misprijst? Gij hebt te beslissen, niet ik; Spreek dus uit, wat ge meent!
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Verstandige mensen zullen mij zeggen, Met den wijzen man, die mij hoort:
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Job heeft niet verstandig gesproken, Zijn rede getuigt niet van inzicht.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Waarachtig, Job zal ten einde toe worden beproefd, Om zijn antwoorden, boosdoeners waardig;
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Want hij heeft bij zijn zonde de misdaad gevoegd, Ons te honen, en tegen God een grote mond op te zetten!