< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Але слухай но, Йо́ве, промови мої, і візьми́ до ушей всі слова́ мої.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Ось я уста свої відкрива́ю, в моїх устах говорить язик мій.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Простота́ мого серця — слова́ мої, і ви́словлять ясно знання́ мої уста.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Дух Божий мене учинив, й оживляє мене Всемогутнього по́дих.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Якщо можеш, то дай мені відповідь, ви́шикуйсь передо мною, поста́вся!
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Тож Божий і я, як і ти, — з глини ви́тиснений теж і я!
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Ото страх мій тебе не настра́шить, і не буде тяжко́ю рука моя на тобі.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Отож, говорив до моїх ушей ти, і я чув голос слів:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
„Чистий я, без гріха, я невинний, і немає провини в мені!
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Оце Сам Він причини на мене знахо́дить, уважає мене Собі ворогом.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
У кайда́ни закув мої но́ги, усі стежки́ мої Він стереже“.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Ось у цьому ти не справедливий! Відповім я тобі, бо більший же Бог за люди́ну!
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Чого Ти із Ним спереча́єшся, що про всі Свої справи Він відповіді не дає?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
Бо Бог промовляє і раз, і два ра́зи, та люди́на не бачить того́:
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
у сні, у виді́нні нічно́му, коли міцний сой на людей напада́є, в дрімо́тах на ложі, —
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
тоді відкриває Він ухо людей, і настра́шує їх осторо́гою,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
щоб відве́сти люди́ну від чину її́, і Він гордість від мужа ховає,
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
щоб від гро́бу повстримати душу його́, а живая його щоб не впала на ра́тище.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
І карається хворістю він на посте́лі своїй, а в костя́х його сва́рка міцна́.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
І жива його бри́диться хлібом, а душа його — стравою влю́бленою.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
Гине тіло його, аж не видно його, і вистають його кості, що пе́рше не видні були́.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
І до гро́бу душа його збли́жується, а живая його — до померлих іде.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Якщо ж Ангол-засту́пник при нім, один з тисячі, щоб предста́вити люди́ні її правоту,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
то Він буде йому милосердний та й скаже: „Звільни ти його, щоб до гро́бу не йшов він, — Я ви́куп знайшов“.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
Тоді відмоло́диться тіло його, пове́рне до днів його ю́ности.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
Він благатиме Бога, й його Собі Він уподо́бає, і обличчя його буде бачити з окликом радости, і чоловікові верне його справедливість.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
Він диви́тиметься на людей й говоритиме: „Я грішив був і правду кривив, та мені не відплачено.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Він викупив душу мою, щоб до гро́бу не йшла, і буде бачити світло живая моя“.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Бог робить це все дві́чі-три́чі з люди́ною,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
щоб душу її відвернути від гро́бу, щоб він був освітлений світлом живих.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Уважай, Йове, слухай мене, мовчи, а я промовля́тиму!
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
Коли маєш слова́, то дай мені відповідь, говори, бо бажаю твого оправда́ння.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
Якщо ні — ти послухай мене; помовчи, й я навчу́ тебе мудрости!“

< Yobu 33 >