< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
[Audi igitur, Job, eloquia mea, et omnes sermones meos ausculta.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Ecce aperui os meum: loquatur lingua mea in faucibus meis.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Simplici corde meo sermones mei, et sententiam puram labia mea loquentur.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Spiritus Dei fecit me, et spiraculum Omnipotentis vivificavit me.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Si potes, responde mihi, et adversus faciem meam consiste.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Ecce, et me sicut et te fecit Deus, et de eodem luto ego quoque formatus sum.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Verumtamen miraculum meum non te terreat, et eloquentia mea non sit tibi gravis.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Dixisti ergo in auribus meis, et vocem verborum tuorum audivi:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
Mundus sum ego, et absque delicto: immaculatus, et non est iniquitas in me.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Quia querelas in me reperit, ideo arbitratus est me inimicum sibi.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
Posuit in nervo pedes meos; custodivit omnes semitas meas.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Hoc est ergo in quo non es justificatus: respondebo tibi, quia major sit Deus homine.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Adversus eum contendis, quod non ad omnia verba responderit tibi?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
Semel loquitur Deus, et secundo idipsum non repetit.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
Per somnium, in visione nocturna, quando irruit sopor super homines, et dormiunt in lectulo,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
tunc aperit aures virorum, et erudiens eos instruit disciplina,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
ut avertat hominem ab his quæ facit, et liberet eum de superbia,
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
eruens animam ejus a corruptione, et vitam illius ut non transeat in gladium.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
Increpat quoque per dolorem in lectulo, et omnia ossa ejus marcescere facit.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
Abominabilis ei fit in vita sua panis, et animæ illius cibus ante desiderabilis.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
Tabescet caro ejus, et ossa, quæ tecta fuerant, nudabuntur.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
Appropinquavit corruptioni anima ejus, et vita illius mortiferis.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Si fuerit pro eo angelus loquens, unus de millibus, ut annuntiet hominis æquitatem,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
miserebitur ejus, et dicet: Libera eum, ut non descendat in corruptionem: inveni in quo ei propitier.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
Consumpta est caro ejus a suppliciis: revertatur ad dies adolescentiæ suæ.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
Deprecabitur Deum, et placabilis ei erit: et videbit faciem ejus in jubilo, et reddet homini justitiam suam.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
Respiciet homines, et dicet: Peccavi, et vere deliqui, et ut eram dignus, non recepi.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Liberavit animam suam, ne pergeret in interitum, sed vivens lucem videret.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Ecce hæc omnia operatur Deus tribus vicibus per singulos,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
ut revocet animas eorum a corruptione, et illuminet luce viventium.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Attende, Job, et audi me: et tace, dum ego loquor.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
Si autem habes quod loquaris, responde mihi: loquere, volo enim te apparere justum.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
Quod si non habes, audi me: tace, et docebo te sapientiam.]

< Yobu 33 >