< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Atòkile, Jòb, tanpri, koute sa m'ap di ou. Louvri zòrèy ou byen pou ou tande m'.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
M' pare pou m' di dènye sa ki vin nan bouch mwen.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
M' pral di tou sa ki nan kè m'. Se verite a tou senp mwen pral pale.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Se lespri Bondye a ki fè m'. Se souf Bondye ki gen tout pouvwa a ki ban m' lavi.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Si ou kapab, w'a reponn mwen. Pare kò ou. Pran pozisyon batay ou avè m'.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Ou menm avè m', devan Bondye nou tout se menm. Nou tou de, se ak labou li fè nou.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Ou wè! Ou pa bezwen pè m'! Mwen pa ka fè ou anyen!
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Mwen te tande ou ak de zòrèy mwen. Ki jan ou fè ka di:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
Mwen menm, mwen inonsan. M' pa fè ankenn peche! M' pa gen anyen sou konsyans mwen.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Men, se Bondye ki pretann mwen ba l' jwen pou l' atake m'. Se li menm k'ap aji avè m' tankou si mwen te lènmi l'.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
Li mete de pye m' nan sèp. L'ap veye tou sa m'ap fè.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
La, Jòb monchè, m'ap reponn ou: ou antò. Paske Bondye pa kanmarad moun.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Poukisa w'ap chache Bondye kont konsa? Se paske li pa reponn lè w'ap plenyen nan pye l'?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
Bondye pale divès jan. Men, pesonn pa okipe sa l'ap di.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
Lè moun kouche nan kabann yo, lè yo fon nan dòmi lannwit, Bondye pale ak yo nan rèv, nan vizyon.
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
Li fè yo konnen sa li gen pou l' di yo. Li ba yo avètisman pou yo mache sou piga yo.
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
Li vle pou yo kite move chemen y'ap swiv la, pou yo pa kite lògèy vire tèt yo.
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
Konsa, yo p'ap mouri. Y'a sove lavi yo.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
Bondye avèti moun tou lè li voye maladi sou yo. Li ba yo doulè nan tout kò yo.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
Li bay yo degoutans manje. Yo pèdi anvi manje menm lò manje a gou.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
Y'ap depafini, tout moun wè jan y'ap vin mèg. Tout zo nan kò yo griyen.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
Sa ki rete pou yo mouri a, pou y' ale nan peyi san chapo a pa anyen.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Lè sa a, yon zanj Bondye ka vin bò kote l', yonn nan milyonven zanj Bondye yo ki la pou fè moun chonje devwa yo.
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
Zanj lan va gen pitye pou li. L'a di Bondye: -Tanpri, pa kite l' mouri. M'ap peye pou sove lavi li.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
Kò li va refè, l'a vin fre tankou lè l' te jenn.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
Li lapriyè Bondye, Bondye reponn li. li al adore Bondye ak kè kontan. Bondye padonnen l' devan tout moun.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
L'ap mache bay Bondye lwanj toupatou. L'ap di: -Mwen te peche, mwen te fè sa ki mal. Men, Bondye pa fè m' peye pou sa m' te fè a.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Li egzante m' lanmò. Li ban m' lavi ankò.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Men tou sa Bondye ap fè, de fwa, twa fwa pou lèzòm,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
pou l' pa kite yo mouri, pou l' ba yo lavi ak kè kontan.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Koulye a, Jòb, louvri zòrèy ou! Koute byen sa m'ap di! Pe bouch ou la! Kite m' fin pale!
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
Men, si ou gen kichòy ou vle di, pale; m'ap koute ou. Paske mwen ta vle ba ou rezon.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
Osinon, pe bouch ou, koute m' pito! Kite m' moutre ou sa ki rele gen bon konprann.

< Yobu 33 >