< Yobu 33 >
1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Cependant Job écoute mes paroles, prête une oreille attentive à ce que je vais dire.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Tu vois j'ouvre la bouche et ma langue se meut.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
La pureté de mon cœur se manifestera en mes discours; mes lèvres ne laisseront passer que des sentences irréprochables.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
L'esprit divin m'anime; le souffle du Tout-Puissant m'a instruit.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Tu me répondras, si tu le peux; attends et tenons-nous face à face.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Je suis comme toi formé de boue; nous provenons du même Créateur.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Je ne veux ni me faire craindre, ni te troubler; ma main ne te sera pas pesante.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Je n'ai rien perdu de ta défense, mes oreilles l'ont recueillie tout entière; tu as dit:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
Je suis pur, je ne pèche point; je suis irréprochable, car j'observe les lois.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Dieu a trouvé sujet de m'accuser; il m'a jugé comme un ennemi.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
Il a mis mon pied dans une entrave; il a posé des sentinelles sur toutes mes voies.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Comment as-tu osé dire: Je suis juste et Dieu ne m'a pas exaucé? L'Eternel n'est-il pas au-dessus de tous les humains?
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Tu as dit: Pourquoi Dieu n'a-t-il pas écouté un seul mot de ma cause?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
Ce que le Seigneur a dit une fois, il le répète encore.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
En nos songes ou dans nos méditations nocturnes, à l'heure où les hommes assoupis sur leur couche ressentent une terreur surnaturelle,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
Il découvre leurs pensées; il donne une forme à leurs craintes secrètes; il les épouvante;
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
Il les détourne de l'iniquité; il préserve leur corps de la chute.
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
A de tels humains, il a déjà sauvé la vie; il l'a empêché de succomber dans les batailles.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
Pour le blâmer derechef, il l'étend malade sur son lit; il engourdit tous ses os.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
Et l'homme ne peut goûter d'aucun aliment; et son âme en désirera,
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
Jusqu'à ce que ses chairs pourrissent et que ses os vides de mœlle se montrent à nu.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
Son âme s'est approchée de la mort et sa vie de l'enfer. ()
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Mais, y eût-il là mille anges exterminateurs, pas un seul ne le blessera, si son cœur songe à se convertir à Dieu: le Seigneur lui fera connaître ce qu'il lui reproche; il lui montrera sa folie;
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
Il empêchera la mort de le saisir; il renouvellera son corps comme l'enduit d'un mur; il remplira ses os de mœlle;
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
Il lui rendra des chairs délicates comme celles d'un enfant; il lui rendra sa virilité parmi les hommes.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
Ses prières au Seigneur seront exaucées; il verra le front serein, les manifestations de Dieu; il rendra justice à ses semblables.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
Alors il se fera des reproches en lui-même, disant: Qu'ai-je fait? Je n'ai point été puni comme le méritaient mes péchés.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Mon Dieu, préservez mon âme d'entrer dans la perdition, et ma vie verra la lumière.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Voilà donc ce que, de trois manières, le Tout-Puissant fait pour chacun des mortels.
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
C'est lui qui a protégé mon âme contre la mort, afin qu'à la lumière, ma vie chante ses louanges.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Prête l'oreille, Job; écoute-moi, garde le silence, c'est à moi seul de parler.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
Cependant, si tu as de bonnes raisons, réponds-moi; parle, je veux avec toi être juste;
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
Sinon, écoute; garde le silence et je t'instruirai.