< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Howbeit, Job, I pray thee, hear my speech, and hearken to all my words.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Behold now, I have opened my mouth, my tongue hath spoken in my mouth.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
My words [shall utter] the uprightness of my heart: and that which my lips know they shall speak sincerely.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
The spirit of God hath made me, and the breath of the Almighty giveth me life.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
If thou canst, answer thou me; set [thy words] in order before me, stand forth.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Behold, I am toward God even as thou art: I also am formed out of the clay.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Behold, my terror shall not make thee afraid, neither shall my pressure be heavy upon thee.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Surely thou hast spoken in mine hearing, and I have heard the voice of [thy] words, [saying],
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
I am clean, without transgression; I am innocent, neither is there iniquity in me:
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Behold, he findeth occasions against me, he counteth me for his enemy;
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
He putteth my feet in the stocks, he marketh all my paths.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Behold, I will answer thee, in this thou art not just; for God is greater than man.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Why dost thou strive against him? for he giveth not account of any of his matters.
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
For God speaketh once, yea twice, [though man] regardeth it not.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
In a dream, in a vision of the night, when deep sleep falleth upon men, in slumberings upon the bed;
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
Then he openeth the ears of men, and sealeth their instruction,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
That he may withdraw man [from his] purpose, and hide pride from man;
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
He keepeth back his soul from the pit, and his life from perishing by the sword.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
He is chastened also with pain upon his bed, and with continual strife in his bones:
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
So that his life abhorreth bread, and his soul dainty meat.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
His flesh is consumed away, that it cannot be seen; and his bones that were not seen stick out.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
Yea, his soul draweth near unto the pit, and his life to the destroyers.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
If there be with him an angel, an interpreter, one among a thousand, to shew unto man what is right for him;
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
Then he is gracious unto him, and saith, Deliver him from going down to the pit, I have found a ransom.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
His flesh shall be fresher than a child’s; he returneth to the days of his youth:
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
He prayeth unto God, and he is favourable unto him; so that he seeth his face with joy: and he restoreth unto man his righteousness.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
He singeth before men, and saith, I have sinned, and perverted that which was right, and it profited me not:
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
He hath redeemed my soul from going into the pit, and my life shall behold the light.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Lo, all these things doth God work, twice, [yea] thrice, with a man,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
To bring back his soul from the pit, that he may be enlightened with the light of the living.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Mark well, O Job, hearken unto me: hold thy peace, and I will speak.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
If thou hast any thing to say, answer me: speak, for I desire to justify thee.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
If not, hearken thou unto me: hold thy peace, and I will teach thee wisdom.

< Yobu 33 >