< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
“And yet, please, O Job, Hear my speech and give ear [to] all my words.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Now behold, I have opened my mouth, My tongue has spoken in the palate.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Of the uprightness of my heart [are] my sayings, And my lips have clearly spoken knowledge.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
The Spirit of God has made me, And the breath of the Mighty quickens me.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
If you are able—answer me, Set in array before me—station yourself.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Behold, I [am], according to your word, for God, I have also been formed from the clay.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Behold, my terror does not frighten you, And my burden on you is not heavy.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Surely you have spoken in my ears, And the sounds of words I hear:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
I [am] pure, without transgression, I [am] innocent, and I have no iniquity.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Behold, He develops hindrances against me, He reckons me for an enemy to Him,
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
He puts my feet in the stocks, He watches all my paths.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Behold, you have not been righteous [in] this, I answer you, that God is greater than man.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Why have you striven against Him, When [for] all His matters He does not answer?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
For once God speaks, and twice (he does not behold it),
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
In a dream—a vision of night, In the falling of deep sleep on men, In slumberings on a bed.
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
Then He uncovers the ear of men, And seals for their instruction,
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
To turn aside man [from] doing, And He conceals pride from man.
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
He keeps back his soul from corruption, And his life from passing away by a dart.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
And he has been reproved With pain on his bed, And the strife of his bones [is] enduring.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
And his life has nauseated bread, And his soul desirable food.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
His flesh is consumed from being seen, And his bones are high, they were not seen!
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
And his soul draws near to the pit, And his life to those causing death.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
If there is a messenger by him, An interpreter—one of a thousand, To declare for man his uprightness,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
Then He favors him and says, Ransom him from going down to the pit, I have found an atonement.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
Fresher [is] his flesh than a child’s, He returns to the days of his youth.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
He makes supplication to God, And He accepts him. And he sees His face with shouting, And He returns to man His righteousness.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
[Then] he looks on men and says, I sinned, and I have perverted uprightness, And it has not been profitable to me.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
He has ransomed my soul From going over into the pit, And my life looks on the light.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Behold, God works all these, Twice, [even] three times with man,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
To bring back his soul from the pit, To be enlightened with the light of the living.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Attend, O Job, listen to me, Keep silent, and I speak.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
If there are words—answer me, Speak, for I have a desire to justify you.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
If there are not—listen to me, Keep silent, and I teach you wisdom.”

< Yobu 33 >