< Yobu 33 >
1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Howbeit hear, Job, my words, and hearken to my speech.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
For behold, I have opened my mouth, and my tongue has spoken.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
My heart [shall be found] pure by [my] words; and the understanding of my lips shall meditate purity.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
The Divine Spirit is that which formed me, and the breath of the Almighty that which teaches me.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
If thou canst, give me an answer: wait therefore; stand against me, and I [will stand] against thee.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Thou art formed out of the clay as also I: we have been formed out of the same [substance].
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
My fear shall not terrify thee, neither shall my hand be heavy upon thee.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
But thou hast said in mine ears, (I have heard the voice of thy words; ) because thou sayest, I am pure, not having sinned;
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
I am blameless, for I have not transgressed.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Yet he has discovered a charge against me, and he has reckoned me as an adversary.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
And he has put my foot in the stocks, and has watched all my ways.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
For how sayest thou, I am righteous, yet he has not hearkened to me? for he that is above mortals is eternal.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
But thou sayest, Why has he not heard every word of my cause?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
For when the Lord speaks once, or a second time,
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
[sending] a dream, or in the meditation of the night; (as when a dreadful alarm happens to fall upon men, in slumberings on the bed: )
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
then opens he the understanding of men: he scares them with such fearful visions:
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
to turn a man from unrighteousness, and he delivers his body from a fall.
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
He spares also his soul from death, and [suffers] him not to fall in war.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
And again, he chastens him with sickness on his bed, and the multitude of his bones is benumbed.
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
And he shall not be able to take any food, though his soul shall desire meat;
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
until his flesh shall be consumed, and he shall shew his bones bare.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
His soul also draws nigh to death, and his life is in Hades.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Though there should be a thousand messengers of death, not one of them shall wound him: if he should purpose in his heart to turn to the Lord, and declare to man his fault, and shew his folly;
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
he will support him, that he should not perish, and will restore his body as [fresh] plaster upon a wall; and he will fill his bones with morrow.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
And he will make his flesh tender as that of a babe, and he will restore him among men in [his] full strength.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
And he shall pray to the Lord, and his prayer shall be accepted of him; he shall enter with a cheerful countenance, with a full expression [of praise]: for he will render to men [their] due.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
Even then a man shall blame himself, saying, What kind of things have I done? and he has not punished me according to the full amount of my sins.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Deliver my soul, that it may not go to destruction, and my life shall see the light.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Behold, all these things, the Mighty One works in a threefold manner with a man.
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
And he has delivered my soul from death, that my life may praise him in the light.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Hearken, Job, and hear me: be silent, and I will speak.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
If thou hast words, answer me: speak, for I desire thee to be justified.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
If not, do thou hear me: be silent, and I will teach thee.