< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
Og Job, hør dog nu min Tale, og vend dine Øren til alle mine Ord!
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Se nu, jeg har opladt min Mund, min Tunge taler allerede ved min Gane.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
Mine Taler skulle udsige mit Hjertes Oprigtighed, og mine Læber skulle udtale rent det, som jeg ved.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
Guds Aand har skabt mig, og den Almægtiges Aande gør mig levende.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
Dersom du kan, saa giv mig Svar; rust dig for mit Ansigt og fremstil dig!
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Se, jeg er ligesom du over for Gud, ogsaa jeg er dannet af Ler.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Se, Rædsel for mig skal ikke forfærde dig, og intet Tryk fra mig skal være svart over dig.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Men du sagde for mine Øren, og jeg hørte Talen, som lød:
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
Jeg er ren, uden Overtrædelse, jeg er skyldfri, og der er ingen Misgerning hos mig.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Se, han har fundet paa Fjendtligheder imod mig, han agter mig for sin Modstander;
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
han har lagt mine Fødder i Stok, han tager Vare paa alle mine Stier.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Se, heri har du ikke Ret! jeg vil svare dig; thi Gud er for høj for et Menneske.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Hvorfor har du trættet med ham, fordi han ikke gør dig Regnskab for nogen af sine Gerninger?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
Men Gud taler een Gang og anden Gang; man agter ikke derpaa.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
I Drøm, i Syn om Natten, naar den dybe Søvn falder paa Folk, naar de slumre paa Sengen,
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
da aabner han Menneskenes Øren, og besegler Formaningen til dem
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
for at bortdrage Mennesket fra hans Idrætter og for at fjerne Hovmodet fra Manden,
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
for at spare hans Sjæl fra Graven og hans Liv fra at omkomme ved Sværd.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
Han straffes ogsaa med Pine paa sit Leje og med vedholdende Uro i hans Ben,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
saa at hans Liv væmmes ved Brød og hans Sjæl ved lækker Mad;
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
hans Kød fortæres, saa man ikke kan se det, og hans Ben hensmuldre og ses ikke;
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
og hans Sjæl kommer nær til Graven og hans Liv nær til de dræbende Magter.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
Dersom der da er en Engel, en Talsmand, hos ham, en af de tusinde, til at kundgøre Mennesket hans rette Vej:
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
Saa skal Gud forbarme sig over ham og sige: Befri ham, at han ikke farer ned i Graven; jeg har faaet Løsepenge;
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
da skal hans Kød blive kraftigt mere end i den unge Alder; sin Ungdoms Dage skal han faa igen.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
Han skal bede til Gud, og denne skal være ham naadig, og han skal se hans Ansigt med Frydeskrig, og han skal gengive Mennesket hans Retfærdighed.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
Han skal synge for Mennesker og sige: Jeg har syndet og forvendt Retten; men det er ikke blevet mig gengældt.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
Han har befriet min Sjæl, at den ikke farer ned i Graven, og mit Liv skal se paa Lyset.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Se, alle disse Ting gør Gud to, tre Gange ved en Mand
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
for at føre hans Sjæl tilbage fra Graven, at den maa beskinnes af de levendes Lys.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Mærk det, Job! hør mig; ti stille, og jeg vil tale.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
Har du noget at sige, da giv mig Svar; tal, thi jeg har Lyst til at give dig Ret.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
Men har du intet, da hør du paa mig; ti stille, saa vil jeg lære dig Visdom!

< Yobu 33 >