< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
І переста́ли ті троє мужів відповідати Йову, бо він був справедливий в оча́х своїх.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
І запалився гнів Елігу, сина Барах'їлового, бузянина, з роду Рамового, — на Йова запали́вся гнів його за те, що той уважав душу свою справедливішою за Бога.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Також на трьох при́ятелів його запалився його гнів за те, що не знайшли вони відповіді, а зробили тільки Йова винним.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
А Елігу вичікував Йова та їх із словами, бо вони були ста́рші віком за нього.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
І побачив Елігу, що нема належної відповіді в устах тих трьох людей, — і запалився його гнів!
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
І відповів бузянин Елі́гу, син Барах'їлів, та й сказав: „Молодий я літа́ми, ви ж ста́рші, тому́ то я стри́мувався та боявся знання́ своє ви́словити вам
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Я поду́мав: Хай вік промовля́є, і хай розуму вчить многолі́ття!
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Справді, дух — він у люди́ні, та Всемогутнього по́дих їх мудрими чинить.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Многолі́тні не за́вжди розумні, і не все розуміються в праві старі́.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Тому́ я кажу: Послухай мене, — хай знання́ своє ви́словлю й я!
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Тож слів ваших вичі́кував я, наставляв свої уші до вашої мудрости, поки справу ви дослідите́.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
І я приглядався до вас, й ось немає між вами, хто б Йо́ву довів, хто б відповідь дав на слова́ його!
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Щоб ви не сказали: „Ми мудрість знайшли: не люди́на, а Бог перемо́же його́!“
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Не на мене слова́ він скеро́вував, і я не відповім йому мовою вашою.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Полякались вони, вже не відповіда́ють, не мають вже слів,
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Я чекав, що не бу́дуть вони говорити, що спини́лись, не відповідають уже.
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Відповім також я свою ча́стку, і ви́словлю й я свою ду́мку.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Бо я повний слова́ми, — дух мойо́го нутра́ докуча́є мені.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Ось утро́ба моя, мов вино невідкри́те, — вона трі́скається, як нові бурдюки́!
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Нехай я скажу́ — й буде легше мені, нехай у́ста відкрию свої — й відповім!
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
На осо́бу не бу́ду уваги звертати, не буду підле́щуватись до люди́ни,
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
бо не вмію підле́щуватись! Коли ж ні, — нехай зараз ві́зьме мене мій Творе́ць!

< Yobu 32 >