< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Así que estos tres hombres no dieron más respuestas a Job, porque él parecía tener razón.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Y Eliu, el hijo de Baraquel el Buzita, de la familia de Ram, estaba enojado, ardiendo de ira contra Job, porque se parecía a sí mismo más justo que Dios;
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Y estaba enojado con sus tres amigos, porque no habían podido darle una respuesta, y no habían dejado claro el pecado de Job.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Ahora Eliú había guardado silencio mientras Job estaba hablando, porque eran más viejos que él;
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Y cuando Eliu vio que no había respuesta en la boca de los tres hombres, se enojó mucho.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Y Eliú, el hijo de Baraquel el Buzita, respondió y dijo: Soy joven, y tú eres muy viejo, así que tenía miedo, y evité poner mi conocimiento delante de ti.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Me dije a mí mismo: que los días hablarán y que muestren su sabiduría los muchos en años.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Pero en verdad es el espíritu del Todopoderoso en el hombre, lo que les da conocimiento.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
No son los viejos los que son sabios, y los que están llenos de años no tienen el conocimiento de lo que es correcto.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Por eso digo: “Escúchame, y expondré mi conocimiento”.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Esperaba tus palabras, escuchaba tus sabios dichos; mientras estabas buscando qué decir,
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Estaba tomando nota; y verdaderamente ninguno de ustedes pudo aclarar el error de Job, o dar una respuesta a sus palabras.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Cuida de no decir: Hemos encontrado la sabiduría; Dios puede vencerlo, pero no el hombre.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
No propondré palabras como éstas, ni haré uso de tus palabras para responderle.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
El miedo los ha vencido, no tienen más respuestas que dar; Han llegado a su fin.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
¿Y voy a seguir esperando mientras no tienen nada que decir? ¿Mientras se callan y no dan más respuestas?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Daré mi respuesta; Voy a presentar mis conocimientos.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Porque estoy lleno de palabras, el espíritu dentro de mi me constriñe.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Mi estómago es como el vino que no puede salir; Como las pieles llenas de vino nuevo, casi se rompe.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Déjame decir lo que tengo en mente, para que pueda consolarme; Déjame contestar con la boca abierta.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
No permitas que respete a ningún hombre, o que le dé nombres de honor a ningún ser vivo.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
Porque no puedo dar nombres de honor a ningún hombre; y si lo hiciera, mi Creador me llevaría rápidamente.

< Yobu 32 >